Yeremiya 20:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Koma Yehova anali nane+ ngati msilikali wamphamvu ndi woopsa.+ N’chifukwa chake anthu amene akundizunza adzakhumudwa ndipo sadzapambana.+ Adzachita manyazi kwambiri chifukwa adzaona kuti sizinawayendere bwino. Manyazi awo adzakhala nawo mpaka kalekale ndipo sadzaiwalika.+ Ezekieli 3:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Koma ndachititsa nkhope yako kuti ikhale yolimba mofanana ndi nkhope zawo,+ ndiponso chipumi chako kuti chikhale cholimba mofanana ndi zipumi zawo.+ Mika 3:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Koma ine ndili ndi mphamvu zochuluka chifukwa cha mzimu wa Yehova. Ndine wokonzeka kuchita zachilungamo ndi kusonyeza mphamvu+ kuti ndiuze mbadwa za Yakobo za kupanduka kwawo, komanso kuti ndiuze Isiraeli za tchimo lake.+
11 Koma Yehova anali nane+ ngati msilikali wamphamvu ndi woopsa.+ N’chifukwa chake anthu amene akundizunza adzakhumudwa ndipo sadzapambana.+ Adzachita manyazi kwambiri chifukwa adzaona kuti sizinawayendere bwino. Manyazi awo adzakhala nawo mpaka kalekale ndipo sadzaiwalika.+
8 Koma ndachititsa nkhope yako kuti ikhale yolimba mofanana ndi nkhope zawo,+ ndiponso chipumi chako kuti chikhale cholimba mofanana ndi zipumi zawo.+
8 Koma ine ndili ndi mphamvu zochuluka chifukwa cha mzimu wa Yehova. Ndine wokonzeka kuchita zachilungamo ndi kusonyeza mphamvu+ kuti ndiuze mbadwa za Yakobo za kupanduka kwawo, komanso kuti ndiuze Isiraeli za tchimo lake.+