Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 23:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 “Tsoka abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pamalo anga odyetsera ziweto!”+ watero Yehova.

  • Mika 3:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ine ndinapitiriza kunena kuti: “Tamverani inu atsogoleri a mbadwa za Yakobo ndi inu olamulira a nyumba ya Isiraeli.+ Kodi si inu oyenera kudziwa chilungamo?+

  • Mika 3:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Atsogoleri a mumzindawo saweruza asanalandire chiphuphu+ ndipo ansembe ake amaphunzitsa kuti apeze malipiro.+ Aneneri ake amalosera kuti apeze ndalama.+ Komatu iwo amadalira Yehova ndipo amanena kuti: “Kodi Yehova sali pakati pathu?+ Choncho tsoka silidzatigwera.”+

  • Zefaniya 3:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Akalonga ake anali mikango imene inali kubangula.+ Oweruza ake anali mimbulu yoyenda usiku imene sinatafune mafupa mpaka m’mawa.+

  • Zekariya 11:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Tsoka m’busa wanga wopanda pake+ amene akusiya nkhosa.+ Lupanga lidzamutema padzanja ndi kuboola diso lake la kudzanja lamanja. Dzanja lake lidzafota,+ ndipo diso lake la kudzanja lamanja lidzachita mdima.”

  • Mateyu 23:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Tsoka kwa inu alembi ndi Afarisi, onyenga inu! Chifukwa mukutseka+ ufumu wakumwamba kuti anthu asalowemo. Pakuti inuyo+ simukulowamo, mukuletsa amene akufuna kulowamo kuti asalowe.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena