Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 23:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Kenako inaitanitsa ansembe onse kuchokera m’mizinda ya Yuda. Inawaitanitsa kuti isandutse malo okwezeka kukhala osayenera kulambirako, kumene ansembewo ankafukizako nsembe yautsi, kuyambira ku Geba+ mpaka ku Beere-seba.+ Inagwetsa malo okwezeka a pazipata amene anali pakhomo la pachipata cha Yoswa mkulu wa mzindawo. Chipata cha Yoswacho chinali mbali ya kumanzere munthu akamalowa pachipata cha mzindawo.

  • 2 Mbiri 29:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Ndiyeno anawauza kuti: “Tamverani Alevi inu. Dziyeretseni+ ndipo muyeretsenso nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Mutulutse chinthu chodetsedwa m’malo oyera.+

  • Nehemiya 9:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Mafumu athu, akalonga athu, ansembe athu ndi makolo athu+ sanatsatire chilamulo chanu+ ndipo sanamvere malamulo anu+ kapena zikumbutso zanu zowachenjeza.+

  • Yeremiya 23:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Aneneri ndi ansembe, onse aipitsidwa+ ndipo m’nyumba mwanga ndapezamo zoipa zimene akuchita,”+ watero Yehova.

  • Ezekieli 8:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndiyeno iye anandiuza kuti: “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Isiraeli akuchita mu mdima?+ Kodi waona zimene aliyense wa iwo akuchita m’chipinda chamkati mmene muli fano lake losema? Iwo akunena kuti, ‘Yehova sakutiona.+ Yehova wachokamo m’dziko muno.’”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena