22 Anthu anga ndi opusa.+ Iwo sanaganizire za ine.+ Iwo ndi ana opanda nzeru ndipo sazindikira kalikonse.+ Iwo ndi anzeru pa kuchita zoipa koma sadziwa kuchita zabwino.+
9 Ndani ali ndi nzeru kuti amvetse zinthu zimenezi?+ Wochenjera ndani kuti adziwe zimenezi?+ Pakuti njira za Yehova ndi zowongoka+ ndipo anthu olungama ndi amene adzayendamo,+ koma olakwa adzapunthwa m’njira zimenezo.+
18 Pamene akuyenda motero, alinso mu mdima wa maganizo,+ otalikirana+ ndi moyo wa Mulungu, chifukwa cha umbuli+ umene uli mwa iwo, chifukwanso cha kukakala+ kwa mitima yawo.