10 Ine Yehova ndimafufuza mtima+ ndi kusanthula impso.+ Munthu aliyense ndimamuchitira zinthu monga mwa zochita zake,+ mogwirizana ndi zipatso za ntchito zake.+
30 “‘Chotero ine ndidzaweruza aliyense wa inu malinga ndi njira zake,+ inu a nyumba ya Isiraeli,’ watero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.+ ‘Lapani ndi kusiya zolakwa zanu zonse+ ndipo musalole kuti chilichonse chizikupunthwitsani ndi kukulakwitsani.+