Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 7:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ndipo munthu akakhudza chodetsa chilichonse, kaya chodetsa cha munthu+ kapena nyama yodetsedwa,+ kapenanso chinthu chilichonse chonyansa chodetsedwa,+ n’kudyako nyama ya nsembe yachiyanjano, imene ndi ya Yehova, munthu wotero aziphedwa kuti asakhalenso pakati pa anthu amtundu wake.’”

  • Numeri 5:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Lamula ana a Isiraeli kuti azitulutsa mumsasa munthu aliyense wakhate,+ aliyense wakukha kumaliseche,+ ndi aliyense wodetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu.+

  • Numeri 9:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Tsopano panali amuna ena amene anadzidetsa pokhudza mtembo wa munthu,+ moti sanathe kukonza nsembe ya pasika pa tsikulo. Chotero anakaonekera kwa Mose ndi Aroni pa tsikulo.+

  • Numeri 19:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Aliyense wokhudza mtembo wa munthu aliyense,+ nayenso azikhala wodetsedwa masiku 7.+

  • Numeri 31:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mumange msasa kunja kwa msasawu, ndipo mukhalemo masiku 7. Aliyense amene wapha munthu,+ ndi aliyense amene wakhudza mtembo wa munthu wophedwa,+ nonsenu, mudziyeretse+ pa tsiku lachitatu ndi pa tsiku la 7. Mudziyeretse limodzinso ndi anthu amene mwawagwirawo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena