Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 34:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Usana ndi usiku, motowo sudzazima. Utsi wake uzidzakwera m’mwamba mpaka kalekale.+ Dzikolo lidzakhala louma ku mibadwomibadwo.+ Mpaka muyaya palibe amene adzadutseko.+

  • Yeremiya 49:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Tsopano amuna inu, tamverani zimene Yehova wasankha kuchitira Edomu+ ndiponso zimene waganiza kuti achitire anthu okhala ku Temani:+ Ndithudi, chilombo chidzakokera ana a nkhosa uku ndi uku, ndipo chidzawononga malo awo okhala chifukwa cha anthuwo.+

  • Ezekieli 25:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndidzatambasulira Edomu+ dzanja langa ndi kupha anthu ndi ziweto m’dzikolo.+ Ndidzalisandutsa bwinja kuyambira ku Temani+ mpaka ku Dedani.+ Iwo adzaphedwa ndi lupanga.

  • Ezekieli 35:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Uuze deralo kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Iwe dera lamapiri la Seiri,+ ine ndithana nawe. Nditambasula dzanja langa ndi kukukhaulitsa.+ Ndikusandutsa bwinja ndiponso malo owonongeka.+

  • Yoweli 3:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Iguputo adzasanduka bwinja,+ Edomu adzasanduka chipululu chopanda kanthu+ chifukwa cha chiwawa chimene anachitira ana a Yuda, ndiponso chifukwa chokhetsa magazi osalakwa m’dziko la Yudalo.+

  • Obadiya 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Chifukwa chakuti m’bale wako Yakobo unam’chitira zachiwawa,+ manyazi adzakugwira.+ Iwe udzawonongedwa ndipo sudzakhalaponso mpaka kalekale.*+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena