Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 27:42
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 42 Pamene Rabeka anauzidwa zimene mwana wake wamkulu Esau ananena, nthawi yomweyo anaitanitsa mwana wake wamng’ono Yakobo n’kumuuza kuti: “M’bale wako Esau akufuna akhazike mtima wake pansi pokubwezera. Iye akufuna kuti akuphe.+

  • Numeri 20:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Koma iye anakanabe, kuti: “Ayi, musadzere+ m’dziko langa.” Mfumu ya Edomu+ itanena zimenezi, inatuluka ndi chikhamu cha anthu, ndi gulu la asilikali lamphamvu, kuti akawathire nkhondo.

  • Salimo 83:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  5 Pakuti ndi mtima wonse, iwo amagawana nzeru,+

      Ndipo anapangana pangano lotsutsana ndi inu.+

  • Salimo 137:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Inu Yehova, kumbukirani+ zimene ana a Edomu+ ananena pa tsiku limene Yerusalemu anawonongedwa,+

      Iwo anati: “Fafanizani mzindawo! Ufafanizeni mpaka pamaziko ake!”+

  • Yoweli 3:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Iguputo adzasanduka bwinja,+ Edomu adzasanduka chipululu chopanda kanthu+ chifukwa cha chiwawa chimene anachitira ana a Yuda, ndiponso chifukwa chokhetsa magazi osalakwa m’dziko la Yudalo.+

  • Amosi 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Yehova wanena kuti, ‘Chifukwa chakuti Edomu wandipandukira mobwerezabwereza,+ sindidzamusinthira chigamulo changa. Sindidzamusinthira chigamulocho chifukwa chakuti anathamangitsa m’bale wake ndi lupanga,+ sanasonyeze chifundo,+ akupitiriza kukhadzulakhadzula zinthu ali wokwiya komanso akukhalabe wokwiya mosalekeza.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena