Yesaya 13:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 “Fuulani, anthu inu,+ chifukwa tsiku la Yehova lili pafupi.+ Lidzabwera ngati kuti Wamphamvuyonse akulanda zinthu.+ Yeremiya 25:33 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 33 Pa tsiku limenelo padzakhala anthu ophedwa ndi Yehova kuchokera kumalekezero a dziko lapansi kufikanso kumalekezero ena a dziko lapansi.+ Sadzawalira maliro, kuwasonkhanitsa pamodzi, kapena kuwaika m’manda.+ Iwo adzakhala ngati manyowa panthaka.’+ Ezekieli 30:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Tsikulo lili pafupi. Inde tsiku la Yehova lili pafupi.+ Limeneli lidzakhala tsiku la mitambo,+ ndiponso nthawi yoikidwiratu yoti mitundu ya anthu iweruzidwe.+ Yoweli 1:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 “Kalanga ine! Tsiku lija likufika.+ Tsiku la Yehova lili pafupi.+ Tsikulo lidzafika ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuyonse. Yoweli 2:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Yehova adzalankhula+ pamaso pa asilikali ake ankhondo+ pakuti anthu a mumsasa wake ndi ambiri.+ Amene akukwaniritsa mawu ake ali ndi mphamvu. Tsiku la Yehova ndi lalikulu+ ndi lochititsa mantha. Ndani angaime pa tsiku limeneli?”+ Zefaniya 1:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Tsiku limenelo ndi tsiku lamkwiyo, tsiku lansautso ndi zowawa,+ tsiku la mphepo yamkuntho ndi losakaza, tsiku lamdima wochititsa mantha,+ tsiku lamitambo yakuda ndi lamdima wandiweyani. 2 Petulo 3:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Muzichita zimenezi poyembekezera+ ndi kukumbukira nthawi zonse kukhalapo kwa tsiku la Yehova,+ pamene kumwamba kudzapsa ndi moto n’kusungunuka,+ ndipo zinthu zimene zimapanga kumwamba ndi dziko lapansi zidzatentha kwambiri n’kusungunuka.
6 “Fuulani, anthu inu,+ chifukwa tsiku la Yehova lili pafupi.+ Lidzabwera ngati kuti Wamphamvuyonse akulanda zinthu.+
33 Pa tsiku limenelo padzakhala anthu ophedwa ndi Yehova kuchokera kumalekezero a dziko lapansi kufikanso kumalekezero ena a dziko lapansi.+ Sadzawalira maliro, kuwasonkhanitsa pamodzi, kapena kuwaika m’manda.+ Iwo adzakhala ngati manyowa panthaka.’+
3 Tsikulo lili pafupi. Inde tsiku la Yehova lili pafupi.+ Limeneli lidzakhala tsiku la mitambo,+ ndiponso nthawi yoikidwiratu yoti mitundu ya anthu iweruzidwe.+
15 “Kalanga ine! Tsiku lija likufika.+ Tsiku la Yehova lili pafupi.+ Tsikulo lidzafika ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuyonse.
11 Yehova adzalankhula+ pamaso pa asilikali ake ankhondo+ pakuti anthu a mumsasa wake ndi ambiri.+ Amene akukwaniritsa mawu ake ali ndi mphamvu. Tsiku la Yehova ndi lalikulu+ ndi lochititsa mantha. Ndani angaime pa tsiku limeneli?”+
15 Tsiku limenelo ndi tsiku lamkwiyo, tsiku lansautso ndi zowawa,+ tsiku la mphepo yamkuntho ndi losakaza, tsiku lamdima wochititsa mantha,+ tsiku lamitambo yakuda ndi lamdima wandiweyani.
12 Muzichita zimenezi poyembekezera+ ndi kukumbukira nthawi zonse kukhalapo kwa tsiku la Yehova,+ pamene kumwamba kudzapsa ndi moto n’kusungunuka,+ ndipo zinthu zimene zimapanga kumwamba ndi dziko lapansi zidzatentha kwambiri n’kusungunuka.