Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Atesalonika 1
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

2 Atesalonika 1:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Ak 1:19

2 Atesalonika 1:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 1:7

2 Atesalonika 1:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1At 1:2
  • +Lu 17:5; 1At 3:12
  • +1At 4:9; 1Pe 1:22

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2005, tsa. 32

2 Atesalonika 1:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Ak 7:14; 1At 2:19
  • +1At 1:6; 2:14; 1Pe 2:21

2 Atesalonika 1:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Chv 16:7
  • +Mac 14:22
  • +Aro 8:17; 2Ti 2:12

2 Atesalonika 1:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 12:19; Chv 6:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 33

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2004, tsa. 19

2 Atesalonika 1:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti “adzaululike.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Lu 17:30; 1Pe 1:7
  • +Mt 25:31; Mko 8:38; Yuda 14

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2004, tsa. 19

    5/1/1993, tsa. 22

2 Atesalonika 1:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ahe 10:30
  • +Yoh 3:19; Aro 1:18
  • +Aro 2:8; Ahe 10:29
  • +1Pe 4:17

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 33

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    9/2019, ptsa. 12-13

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2004, tsa. 19

    5/1/1993, tsa. 22

    5/1/1989, tsa. 19

    1/1/1989, tsa. 20

2 Atesalonika 1:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Pe 2:17; 3:7
  • +Yuda 13
  • +Yes 2:21

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    5/1/1989, tsa. 19

    Kukambitsirana, tsa. 147

2 Atesalonika 1:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 8:17

2 Atesalonika 1:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 8:30; 2Ti 1:9

2 Atesalonika 1:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yoh 17:10; 1Pe 1:7
  • +Yoh 17:21
  • +1Ak 1:4

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

2 Ates. 1:12Ak 1:19
2 Ates. 1:2Aro 1:7
2 Ates. 1:31At 1:2
2 Ates. 1:3Lu 17:5; 1At 3:12
2 Ates. 1:31At 4:9; 1Pe 1:22
2 Ates. 1:42Ak 7:14; 1At 2:19
2 Ates. 1:41At 1:6; 2:14; 1Pe 2:21
2 Ates. 1:5Chv 16:7
2 Ates. 1:5Mac 14:22
2 Ates. 1:5Aro 8:17; 2Ti 2:12
2 Ates. 1:6Aro 12:19; Chv 6:10
2 Ates. 1:7Lu 17:30; 1Pe 1:7
2 Ates. 1:7Mt 25:31; Mko 8:38; Yuda 14
2 Ates. 1:8Ahe 10:30
2 Ates. 1:8Yoh 3:19; Aro 1:18
2 Ates. 1:8Aro 2:8; Ahe 10:29
2 Ates. 1:81Pe 4:17
2 Ates. 1:92Pe 2:17; 3:7
2 Ates. 1:9Yuda 13
2 Ates. 1:9Yes 2:21
2 Ates. 1:10Aro 8:17
2 Ates. 1:11Aro 8:30; 2Ti 1:9
2 Ates. 1:12Yoh 17:10; 1Pe 1:7
2 Ates. 1:12Yoh 17:21
2 Ates. 1:121Ak 1:4
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano (nwt)
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
2 Atesalonika 1:1-12

2 Atesalonika

1 Ine Paulo, pamene ndili limodzi ndi Silivano ndi Timoteyo,+ ndikulembera mpingo wa Atesalonika wogwirizana ndi Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu, kuti:

2 Kukoma mtima kwakukulu, ndi mtendere wochokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu,+ zikhale nanu.

3 Tiyeneradi kumayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu+ abale. N’koyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukula+ kwambiri, ndipo chikondi cha aliyense wa inu kwa mnzake chikuwirikiza.+ 4 Choncho ifeyo timakunyadirani+ ku mipingo ya Mulungu chifukwa cha kupirira kwanu ndi chikhulupiriro chanu pokumana ndi mazunzo ndi masautso onse amene mukulimbana nawo.+ 5 Umenewu ndi umboni wakuti Mulungu amaweruza molungama,+ ndipo chifukwa cha zimenezi mwaonedwa kuti ndinu oyenerera ufumu wa Mulungu,+ umene mukuuvutikira.+

6 Chiweruzo cha Mulunguchi n’cholungama chifukwa akubwezera masautso kwa amene amakusautsani.+ 7 Pa nthawi imene Ambuye Yesu adzaonekere*+ kuchokera kumwamba limodzi ndi angelo ake amphamvu+ m’moto walawilawi, inuyo amene panopo mukuvutika mudzapeza mpumulo pamodzi nafe. 8 Pa nthawi imeneyo adzabwezera chilango+ kwa anthu osadziwa Mulungu+ ndi kwa anthu osamvera uthenga wabwino+ wonena za Ambuye wathu Yesu.+ 9 Amenewa adzawaweruza kuti alandire chilango+ cha chiwonongeko chamuyaya,+ kuwachotsa pamaso pa Ambuye ndi ku ulemerero wa mphamvu zake.+ 10 Adzatero pa nthawi imene adzabwere kudzalandira ulemerero mogwirizana ndi oyera ake.+ Pa tsiku limenelo, onse amene anakhulupirira mwa iye, adzamusirira ndi kumuyang’anitsitsa, chifukwa pakati panu, munakhulupirira umboni umene tinapereka.

11 Pa chifukwa chimenechi, ndithu timakupemphererani nthawi zonse. Timatero kuti Mulungu wathu akuoneni kuti ndinu oyenereradi kuitanidwa ndi iye.+ Mulunguyo achite mokwanira zinthu zonse zabwino zimene akufuna kuchita ndi mphamvu zake, ndipo achititse kuti ntchito zanu zachikhulupiriro zikhale zopindulitsa, 12 kuti dzina la Ambuye wathu Yesu lilemekezeke mwa inu,+ ndi inu mwa iye,+ mogwirizana ndi kukoma mtima kwakukulu+ kwa Mulungu wathu, ndi kwa Ambuye Yesu Khristu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena