Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Nyimbo ya Solomo

    • MSULAMI ALI KU YERUSALEMU (3:6–8:4)

Nyimbo ya Solomo 5:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 4:16
  • +Nym 4:13, 14
  • +Nym 4:11
  • +Nym 1:2

Nyimbo ya Solomo 5:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 3:1
  • +Lu 2:8

Nyimbo ya Solomo 5:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 3:1, 3

Nyimbo ya Solomo 5:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “anandilanda nsalu yanga yofunda kumutu.”

Nyimbo ya Solomo 5:11

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “lili ngati phava la zipatso za kanjedza.”

Nyimbo ya Solomo 5:12

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “Zitakhala mʼmphepete mwa kasupe wa madzi.”

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 30

    11/15/2006, tsa. 19

    11/15/1987, tsa. 25

Nyimbo ya Solomo 5:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 6:2
  • +Nym 1:13

Nyimbo ya Solomo 5:14

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 19

Nyimbo ya Solomo 5:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 92:12

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 19

Nyimbo ya Solomo 5:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:3

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 5:1Nym 4:16
Nyimbo 5:1Nym 4:13, 14
Nyimbo 5:1Nym 4:11
Nyimbo 5:1Nym 1:2
Nyimbo 5:2Nym 3:1
Nyimbo 5:2Lu 2:8
Nyimbo 5:6Nym 3:1, 3
Nyimbo 5:13Nym 6:2
Nyimbo 5:13Nym 1:13
Nyimbo 5:15Sl 92:12
Nyimbo 5:16Nym 2:3
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 5:1-16

Nyimbo ya Solomo

5 “Ndalowa mʼmunda mwanga,+

Iwe mchemwali wanga, mkwatibwi wanga.

Ndathyola mule wanga komanso zonunkhiritsa zanga.+

Ndadya chisa changa cha uchi ndiponso uchi wanga.

Ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.”+

“Idyani, inu anthu okondana!

Imwani ndipo muledzere ndi chikondi chimene mukusonyezana.”+

 2 “Panopa ndili mʼtulo koma mtima wanga uli maso.+

Ndikumva wachikondi wanga akugogoda.”

“Nditsegulire iwe mchemwali wanga, wokondedwa wanga,

Njiwa yanga, iwe wopanda chilema.

Chifukwa mutu wanga wanyowa ndi mame,

Tsitsi langa lopotanapotana, lanyowa ndi chinyezi cha usiku.”+

 3 “‘Ndavula mkanjo wanga.

Kodi ndiuvalenso?

Ndatsuka mapazi anga.

Kodi ndiwadetsenso?’

 4 Wachikondi wanga atachotsa dzanja lake pabowo la chitseko,

Mtima wanga unayamba kugunda chifukwa ndinkafunitsitsa kumuona.

 5 Ndinadzuka kuti ndimutsegulire wachikondi wanga.

Manja anga akuyenderera mule,

Ndiponso zala zanga zikuyenderera mafuta a mule,

Mpaka pahandulo ya loko wachitseko.

 6 Ndinamʼtsegulira wachikondi wanga,

Koma wachikondi wangayo anali atachokapo, atapita.

Ndinadandaula kwambiri atachoka.

Ndinamufunafuna koma sindinamupeze.+

Ndinamuitana koma sanandiyankhe.

 7 Alonda amene ankazungulira mumzinda anandipeza.

Anandimenya ndipo anandivulaza.

Alonda apamipanda anandilanda chofunda changa.*

 8 Ndakulumbiritsani inu ana aakazi a ku Yerusalemu kuti:

Mukamʼpeza wachikondi wanga,

Mumuuze kuti ine chikondi chikundidwalitsa.”

 9 “Kodi wachikondi wakoyo akuposa bwanji achikondi ena onse,

Iwe mkazi wokongola kwambiri kuposa akazi onse?

Kodi wachikondi wakoyo akuposa bwanji achikondi ena onse,

Kuti utilumbiritse lumbiro limeneli?”

10 “Wachikondi wanga ndi wokongola ndipo khungu lake ndi lofiira.

Pa amuna 10,000, iye ndi wooneka bwino kwambiri.

11 Mutu wake ndi wokongola ngati golide, golide wabwino kwambiri.

Tsitsi lake lopotanapotana lili ngati nthambi za kanjedza* zimene zikugwedera,

Ndipo ndi lakuda ngati khwangwala.

12 Maso ake ali ngati njiwa zimene zili pafupi ndi mitsinje yamadzi,

Zimene zikusamba mumkaka,

Zitakhala pafupi ndi damu lodzaza madzi.*

13 Masaya ake ali ngati bedi la maluwa onunkhira,+

Ndiponso ngati munda wa zitsamba zonunkhira umene uli pamalo okwera.

Milomo yake ili ngati maluwa amene akuchucha mafuta a mule.+

14 Zala zake zonenepa bwino ndi zagolide, ndipo zikhadabo zake ndi zakulusolito.

Mimba yake ndi yopangidwa ndi minyanga ya njovu yokutidwa ndi miyala ya safiro.

15 Miyendo yake ili ngati zipilala zamiyala ya mabo zozikidwa pazitsulo zagolide wabwino kwambiri.

Iye ndi wokongola ngati dziko la Lebanoni ndipo ndi wamtali mofanana ndi mitengo ya mkungudza.+

16 Mʼkamwa mwake ndi mokoma kwambiri

Ndipo chilichonse mwa iye nʼchosiririka.+

Ameneyu ndi wachikondi wanga, ameneyu ndi wokondedwa wanga, inu ana aakazi a ku Yerusalemu.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena