Numeri 20:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 “Tenga ndodoyo,+ ndipo iwe ndi m’bale wako Aroni, musonkhanitse khamu lonse la anthuwo. Muuze thanthwe pamaso pawo kuti litulutse madzi. Utulutse madzi m’thanthweli kuti upatse khamulo, kuti limwe limodzi ndi ziweto zawo.”+ Deuteronomo 8:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Mungaiwale amene anakuyendetsani m’chipululu chachikulu ndi chochititsa mantha,+ chokhala ndi njoka zapoizoni,+ zinkhanira ndiponso dziko louma lopanda madzi. Amenenso anakutulutsirani madzi pamwala wolimba ngati nsangalabwi.+ Nehemiya 9:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Munawapatsanso mkate wochokera kumwamba kuti athetse njala yawo.+ Munatulutsa madzi pathanthwe ndi kuwapatsa kuti athetse ludzu lawo,+ ndiyeno munawauza kuti alowe+ ndi kutenga dziko limene munalumbira mutakweza dzanja lanu kuti mudzawapatsa.+ Salimo 78:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Iye anang’amba miyala m’chipululu+Kuti awapatse madzi akumwa ochuluka ngati a m’nyanja.+ Salimo 105:41 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 41 Anatsegula thanthwe ndipo panatuluka madzi ambiri.+Madziwo anayenda ngati mtsinje kudutsa m’dera lopanda madzi.+ Salimo 114:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Amene amasintha thanthwe kukhala dambo la madzi,+Ndiponso amasintha mwala wa nsangalabwi kukhala kasupe.+ Yesaya 48:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Iwo sanamve ludzu+ ngakhale pamene iye anawayendetsa m’chipululu.+ Iye anawatulutsira madzi pathanthwe. Anang’amba thanthwe kuti madzi atulukepo.”+ 1 Akorinto 10:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 ndipo onse anamwa chakumwa chimodzimodzi chauzimu.+ Pakuti anali kumwa pathanthwe lauzimu+ limene linali kuwatsatira, ndipo thanthwelo+ linatanthauza Khristu.+
8 “Tenga ndodoyo,+ ndipo iwe ndi m’bale wako Aroni, musonkhanitse khamu lonse la anthuwo. Muuze thanthwe pamaso pawo kuti litulutse madzi. Utulutse madzi m’thanthweli kuti upatse khamulo, kuti limwe limodzi ndi ziweto zawo.”+
15 Mungaiwale amene anakuyendetsani m’chipululu chachikulu ndi chochititsa mantha,+ chokhala ndi njoka zapoizoni,+ zinkhanira ndiponso dziko louma lopanda madzi. Amenenso anakutulutsirani madzi pamwala wolimba ngati nsangalabwi.+
15 Munawapatsanso mkate wochokera kumwamba kuti athetse njala yawo.+ Munatulutsa madzi pathanthwe ndi kuwapatsa kuti athetse ludzu lawo,+ ndiyeno munawauza kuti alowe+ ndi kutenga dziko limene munalumbira mutakweza dzanja lanu kuti mudzawapatsa.+
41 Anatsegula thanthwe ndipo panatuluka madzi ambiri.+Madziwo anayenda ngati mtsinje kudutsa m’dera lopanda madzi.+
8 Amene amasintha thanthwe kukhala dambo la madzi,+Ndiponso amasintha mwala wa nsangalabwi kukhala kasupe.+
21 Iwo sanamve ludzu+ ngakhale pamene iye anawayendetsa m’chipululu.+ Iye anawatulutsira madzi pathanthwe. Anang’amba thanthwe kuti madzi atulukepo.”+
4 ndipo onse anamwa chakumwa chimodzimodzi chauzimu.+ Pakuti anali kumwa pathanthwe lauzimu+ limene linali kuwatsatira, ndipo thanthwelo+ linatanthauza Khristu.+