Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Oweruza 4:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Pamenepo Debora anati: “Sindilephera, tipitira limodzi. Ngakhale zili choncho, ulemerero sukhala wako kumene ukupitako, chifukwa Yehova adzapereka Sisera m’manja mwa munthu wamkazi.”+ Atatero, Debora ananyamuka n’kutsagana ndi Baraki ku Kedesi.+

  • Oweruza 5:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Kenako anatambasula dzanja lake ndi kugwira chikhomo cha hema.

      Anatambasulanso dzanja lake lamanja ndi kutenga nyundo yamtengo, ya anthu ogwira ntchito mwamphamvu.+

      Atatero anakhoma Sisera m’mutu ndipo chikhomocho chinatulukira mbali ina ya mutu wakewo.+

      Anaphwanya ndi kudula fupa la pafupi ndi khutu la Sisera.

  • 2 Samueli 11:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ndani uja anapha Abimeleki+ mwana wa Yerubeseti?*+ Kodi si mkazi amene anaponya mwala wokhala pamwamba wa mphero+ ali pamwamba pa mpanda, ndipo Abimeleki anafera ku Tebezi+ komweko? N’chifukwa chiyani amuna inu munauyandikira kwambiri mpandawo?’ Pamenepo ukanene kuti, ‘Nayenso Uriya Mhiti, mtumiki wanu, wafa.’”+

  • 2 Samueli 20:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Nthawi yomweyo, mkaziyo anapita mwa nzeru+ zake kwa anthu onse, ndipo anthuwo anadula mutu wa Sheba mwana wa Bikiri ndi kuuponya kwa Yowabu. Zitatero, Yowabu analiza lipenga la nyanga ya nkhosa+ moti anthu onse anabalalika kuchoka kumzindawo ndi kupita kwawo. Yowabu nayenso anabwerera ku Yerusalemu kwa mfumu.

  • Yobu 31:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  3 Kodi si paja wochita zoipa amakumana ndi zosautsa,+

      Ndipo ochitira anzawo zopweteka tsoka limawagwera?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena