-
Yoswa 13:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 (Dera loyambira kukamtsinje kotuluka mu Nailo kum’mawa kwa Iguputo, kukafika kumpoto kumalire ndi Ekironi,+ ankalitcha dziko la Akanani.)+ Madera a Afilisitiwa akulamulidwa ndi olamulira ogwirizana asanu.+ Maderawo ndi Gaza,+ Asidodi,+ Asikeloni,+ Gati+ ndi Ekironi,+ komanso Aavi+ akukhala komweko.
-
-
1 Samueli 6:4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Ndiyeno iwo anafunsa kuti: “Kodi nsembe ya kupalamula imene tiyenera kupereka ikhale chiyani?” Poyankha, ansembe ndi alauli aja anati: “Mupereke zifanizo zisanu zagolide za matenda a mudzi, ndi zifanizo zisanu zagolide za mbewa zoyenda modumpha, malinga ndi chiwerengero cha olamulira ogwirizana+ a Afilisiti. Muchite zimenezi pakuti mliri umene wagwera aliyense wa inu, pamodzi ndi olamulira anu ogwirizana ndi umodzi.
-