Ekisodo 10:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Pamenepo atumiki a Farao anamuuza kuti: “Kodi munthu uyu akhala ngati msampha kwa ife kufikira liti?+ Lolani anthuwa apite kuti akatumikire Yehova Mulungu wawo. Kodi simukudziwabe kuti Iguputo wawonongeka?”+ 1 Samueli 18:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Ndiyeno Sauli anauza Davide kuti: “Mwana wanga wamkazi wamkulu Merabu+ alipo. Ndidzakupatsa ameneyu kuti akhale mkazi wako.+ Koma iwe undisonyeze kulimba mtima kwako ndi kumenya nkhondo za Yehova.”+ Mumtima mwake Sauli anati: “Ndisamuphe ndine ndi dzanja langa, koma amuphe ndi Afilisiti.”+ Salimo 7:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Taonani! Wina ali ndi pakati pa zinthu zoipa,+Watenga pakati pa mavuto ndipo ndithu adzabereka chinyengo.+ Salimo 38:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Anthu amene akufuna kundiwononga anditchera misampha,+Amene akufuna kundivulaza akulankhula motsutsana nane,+Ndipo amakhala akukonza zachinyengo tsiku lonse.+ Miyambo 26:24 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 24 Munthu wodana nawe amadzibisa ndi milomo yake, koma mkati mwake mumakhala chinyengo.+ Yeremiya 9:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Lilime lawo ndiwo muvi wophera anthu.+ Limalankhula chinyengo chokhachokha. Munthu aliyense amalankhula mwamtendere ndi mnzake, koma mumtima mwake amakonza chiwembu.”+
7 Pamenepo atumiki a Farao anamuuza kuti: “Kodi munthu uyu akhala ngati msampha kwa ife kufikira liti?+ Lolani anthuwa apite kuti akatumikire Yehova Mulungu wawo. Kodi simukudziwabe kuti Iguputo wawonongeka?”+
17 Ndiyeno Sauli anauza Davide kuti: “Mwana wanga wamkazi wamkulu Merabu+ alipo. Ndidzakupatsa ameneyu kuti akhale mkazi wako.+ Koma iwe undisonyeze kulimba mtima kwako ndi kumenya nkhondo za Yehova.”+ Mumtima mwake Sauli anati: “Ndisamuphe ndine ndi dzanja langa, koma amuphe ndi Afilisiti.”+
14 Taonani! Wina ali ndi pakati pa zinthu zoipa,+Watenga pakati pa mavuto ndipo ndithu adzabereka chinyengo.+
12 Anthu amene akufuna kundiwononga anditchera misampha,+Amene akufuna kundivulaza akulankhula motsutsana nane,+Ndipo amakhala akukonza zachinyengo tsiku lonse.+
8 Lilime lawo ndiwo muvi wophera anthu.+ Limalankhula chinyengo chokhachokha. Munthu aliyense amalankhula mwamtendere ndi mnzake, koma mumtima mwake amakonza chiwembu.”+