18 “‘Pali ine Mulungu wamoyo, Nebukadirezara adzabwera ndi kuonekera ngati phiri la Tabori+ pakati pa mapiri ena, ndiponso ngati phiri la Karimeli+ m’mphepete mwa nyanja,’ yatero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova wa makamu.+
“Yehova adzabangula ngati mkango mu Ziyoni,+ ndipo adzafuula mu Yerusalemu.+ Malo amene abusa amadyetserako ziweto adzalira, ndipo pansonga ya phiri la Karimeli padzauma.”+