5 koma mudzafunefune malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu onse kuti aikepo dzina lake, kuti lizikhala pamenepo. Amenewo ndiwo malo amene muzidzapitako.+
3 Ndipo Yehova anamuuza kuti: “Ndamva pemphero lako+ ndi pempho lako lopempha chifundo kwa ine. Ndayeretsa+ nyumba imene wamangayi mwa kuikapo dzina langa+ mpaka kalekale, ndipo maso anga+ ndi mtima wanga adzakhala pamenepo nthawi zonse.+