Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 12:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 koma mudzafunefune malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu onse kuti aikepo dzina lake, kuti lizikhala pamenepo. Amenewo ndiwo malo amene muzidzapitako.+

  • 2 Samueli 7:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Iye ndi amene adzamangira dzina langa nyumba,+ ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake wachifumu mpaka kalekale.+

  • 1 Mafumu 8:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Maso anu akhale akuyang’ana+ nyumba ino usiku ndi usana. Akhale akuyang’ana malo amene munanena kuti, ‘Dzina langa lidzakhala kumeneko,’+ kuti mumvere pemphero limene mtumiki wanu akupemphera atayang’ana kumalo ano.+

  • 1 Mafumu 9:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ndipo Yehova anamuuza kuti: “Ndamva pemphero lako+ ndi pempho lako lopempha chifundo kwa ine. Ndayeretsa+ nyumba imene wamangayi mwa kuikapo dzina langa+ mpaka kalekale, ndipo maso anga+ ndi mtima wanga adzakhala pamenepo nthawi zonse.+

  • Salimo 78:68
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 68 Koma anasankha fuko la Yuda,+

      Phiri la Ziyoni limene analikonda.+

  • Salimo 132:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Yehova wasankha Ziyoni,+

      Ndipo amafunitsitsa kuti akhale malo ake okhalamo. Iye amati:+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena