Miyambo 10:19 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 19 Pakachuluka mawu sipalephera kukhala zolakwa,+ koma wodziwa kulamulira milomo yake amachita zinthu mwanzeru.+ Miyambo 12:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Munthu woipa amakodwa ndi kuchimwa kwa milomo yake,+ koma wolungama amachoka m’masautso.+ Miyambo 18:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Pakamwa pa munthu wopusa m’pamene pamamuwononga,+ ndipo milomo yake ndi msampha wa moyo wake.+ Mateyu 12:36 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 36 Ndikukuuzani kuti pa Tsiku la Chiweruzo, anthu adzayankha mlandu pa mawu alionse opanda pake amene iwo amalankhula.+ Yakobo 1:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 Ngati munthu akudziona ngati wopembedza,+ koma salamulira lilime lake,+ ndipo akupitiriza kunyenga mtima wake,+ kupembedza kwa munthu ameneyu n’kopanda pake.+ Yakobo 3:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Pakuti lilime timatamanda nalo Yehova,+ amenenso ndi Atate,+ komanso ndi lilime lomwelo timatemberera+ anthu amene analengedwa “m’chifaniziro cha Mulungu.”+ Yuda 16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Anthu amenewa ndi okonda kung’ung’udza,+ okonda kudandaula za moyo wawo, ongotsatira zilakolako zawo,+ ndipo amalankhula modzitukumula.+ Amatamandanso anthu ena+ n’cholinga choti apezepo phindu.
19 Pakachuluka mawu sipalephera kukhala zolakwa,+ koma wodziwa kulamulira milomo yake amachita zinthu mwanzeru.+
36 Ndikukuuzani kuti pa Tsiku la Chiweruzo, anthu adzayankha mlandu pa mawu alionse opanda pake amene iwo amalankhula.+
26 Ngati munthu akudziona ngati wopembedza,+ koma salamulira lilime lake,+ ndipo akupitiriza kunyenga mtima wake,+ kupembedza kwa munthu ameneyu n’kopanda pake.+
9 Pakuti lilime timatamanda nalo Yehova,+ amenenso ndi Atate,+ komanso ndi lilime lomwelo timatemberera+ anthu amene analengedwa “m’chifaniziro cha Mulungu.”+
16 Anthu amenewa ndi okonda kung’ung’udza,+ okonda kudandaula za moyo wawo, ongotsatira zilakolako zawo,+ ndipo amalankhula modzitukumula.+ Amatamandanso anthu ena+ n’cholinga choti apezepo phindu.