10 Asilikali othamangawo+ anapitiriza ulendo wawo ndipo anapita kumzinda ndi mzinda m’dziko lonse la Efuraimu+ ndi Manase mpaka ku Zebuloni. Koma anthuwo ankangokhalira kuwatonza ndi kuwaseka.+
16 Koma iwo ankangonyogodola+ amithenga a Mulungu woona, kunyoza mawu ake+ ndi kuseka+ aneneri ake, mpaka kufika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa.+ Kenako mkwiyo+ wa Yehova unawagwera.