Yesaya 27:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Chotero zolakwa za Yakobo zidzaphimbidwa mwa njira imeneyi.+ Zimenezi zidzachitika akadzachotsa tchimo lakelo,+ ndiponso akadzasandutsa miyala yonse ya paguwa lansembe kukhala miyala yofewa kwambiri yonyenyekanyenyeka, moti mizati yopatulika+ ndi maguwa ofukizirapo zonunkhira sizidzamangidwanso.+ Ezekieli 36:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 Ine ndidzakuwazani madzi oyera ndipo mudzakhala oyera. Ndidzakuyeretsani+ pokuchotserani zonyansa zanu zonse+ ndi mafano anu onse onyansa.+ Ezekieli 37:23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 23 Iwo sadzadziipitsanso ndi mafano awo onyansa, zinthu zawo zonyansa ndi zochita zawo zonse zophwanya malamulo.+ Ndidzawapulumutsa ku machimo onse amene anali kuchita m’malo awo okhala, ndipo ndidzawayeretsa.+ Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.+ Hoseya 14:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 “Efuraimu adzanena kuti, ‘Kodi mafano ndi a chiyaninso kwa ine?’+ “Ine ndidzamva ndipo ndidzapitirizabe kumuyang’anira.+ Ine ndili ngati mtengo waukulu wa mkungudza wamasamba obiriwira+ ndipo mudzapeza zipatso kwa ine.” Zekariya 13:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Yehova wa makamu wanena kuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathetsa mayina a mafano m’dziko lonseli+ ndipo mafanowo sadzakumbukiridwanso. M’dzikoli ndidzachotsamo aneneri+ komanso mzimu wonyansa.+
9 Chotero zolakwa za Yakobo zidzaphimbidwa mwa njira imeneyi.+ Zimenezi zidzachitika akadzachotsa tchimo lakelo,+ ndiponso akadzasandutsa miyala yonse ya paguwa lansembe kukhala miyala yofewa kwambiri yonyenyekanyenyeka, moti mizati yopatulika+ ndi maguwa ofukizirapo zonunkhira sizidzamangidwanso.+
25 Ine ndidzakuwazani madzi oyera ndipo mudzakhala oyera. Ndidzakuyeretsani+ pokuchotserani zonyansa zanu zonse+ ndi mafano anu onse onyansa.+
23 Iwo sadzadziipitsanso ndi mafano awo onyansa, zinthu zawo zonyansa ndi zochita zawo zonse zophwanya malamulo.+ Ndidzawapulumutsa ku machimo onse amene anali kuchita m’malo awo okhala, ndipo ndidzawayeretsa.+ Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.+
8 “Efuraimu adzanena kuti, ‘Kodi mafano ndi a chiyaninso kwa ine?’+ “Ine ndidzamva ndipo ndidzapitirizabe kumuyang’anira.+ Ine ndili ngati mtengo waukulu wa mkungudza wamasamba obiriwira+ ndipo mudzapeza zipatso kwa ine.”
2 Yehova wa makamu wanena kuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathetsa mayina a mafano m’dziko lonseli+ ndipo mafanowo sadzakumbukiridwanso. M’dzikoli ndidzachotsamo aneneri+ komanso mzimu wonyansa.+