Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 15:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ndi mulungu wina uti amene angafanane nanu, inu Yehova?+

      Ndinu woyera kopambana, ndani angafanane ndi inu?+

      Ndinu woyenera kuopedwa+ ndi kukuimbirani nyimbo zotamanda.+ Inu ndinu wochita zodabwitsa.+

  • Salimo 71:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Inenso ndidzakutamandani ndi chipangizo cha zingwe,+

      Ndidzatamanda choonadi chanu, inu Mulungu.+

      Ndidzaimba nyimbo zokutamandani ndi zeze, Inu Woyera wa Isiraeli.+

  • Yesaya 5:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Chotero monga momwe lawi la moto limanyeketsera mapesi+ komanso monga mmene udzu wouma umanyekera m’malawi a moto, muzu wawo udzawola n’kuyamba kununkha.+ Maluwa awo adzauma n’kuuluzika ngati fumbi, chifukwa akana malamulo a Yehova wa makamu+ ndipo anyoza mawu a Woyera wa Isiraeli.+

  • Yesaya 10:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 M’tsiku limenelo, otsala a Isiraeli+ ndi opulumuka a nyumba ya Yakobo sadzadaliranso yemwe akuwamenya,+ koma ndi mtima wonse adzadalira Yehova, Woyera wa Isiraeli.+

  • Yeremiya 51:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 “Pakuti Mulungu, Yehova wa makamu,+ sanasiye Isiraeli ndi Yuda+ kuti akhale mkazi wamasiye. Dziko la Akasidi lili ndi mlandu waukulu pamaso pa Woyera wa Isiraeli.+

  • Ezekieli 39:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Aisiraeli. Sindidzalolanso kuti dzina langa lidetsedwe,+ ndipo mitundu ina ya anthu idzadziwa kuti ine ndine Yehova,+ Woyera wa ku Isiraeli.’+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena