Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 18:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Choncho anatenga ng’ombe yaing’ono yamphongo imene Eliya anawapatsa, n’kuikonza. Kenako anayamba kuitana dzina la Baala kuyambira m’mawa mpaka masana. Ankaitana kuti: “Inu a Baala, tiyankheni!” Koma sipanamveke mawu alionse,+ ndipo palibe anayankha.+ Iwo anapitiriza kudumphadumpha ngati akuvina, kuzungulira guwa lansembe limene anamanga.

  • Yesaya 37:38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Pamene Senakeribu anali kugwada m’kachisi wa mulungu wake+ Nisiroki,+ ana ake Adarameleki ndi Sarezere anamupha ndi lupanga,+ iwo n’kuthawira kudziko la Ararati.+ Kenako Esari-hadoni+ mwana wake anayamba kulamulira m’malo mwake.

  • Yeremiya 2:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 “Kodi milungu yako imene wadzipangira ili kuti?+ Imeneyo ibwere kwa iwe ngati ingathe kukupulumutsa pa nthawi ya tsoka.+ Pakuti iwe Yuda, milungu yako yachuluka mofanana ndi mizinda yako.+

  • Yona 1:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Zitatero oyendetsa chombo anayamba kuchita mantha ndipo aliyense anayamba kufuulira mulungu wake+ kuti amuthandize. Iwo anayamba kuponya m’nyanja katundu amene anali m’chombomo kuti chipepukidwe.+ Apa n’kuti Yona atatsikira mkatikati mwa chombocho, pakuti chinali ndi zipinda zapansi. Kumeneko Yona anagona tulo tofa nato.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena