Deuteronomo 4:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 ndikutenga kumwamba ndi dziko lapansi+ lero monga mboni zokutsutsani, kuti mudzafafanizidwa mwamsanga m’dziko limene mukupita kukalitenga mutawoloka Yorodano. Simudzatalikitsa masiku anu m’dzikomo chifukwa mudzawonongedwa ndithu.+ Deuteronomo 32:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 32 “Tamverani kumwamba inu, ndiloleni ndilankhule.Ndipo dziko lapansi limve mawu a pakamwa panga.+ Yesaya 1:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Imvani+ kumwamba inu, ndipo tchera khutu iwe dziko lapansi, chifukwa Yehova wanena kuti: “Ndalera ana ndi kuwakulitsa,+ koma iwo andipandukira.+ Yesaya 34:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 34 Mitundu inu, bwerani pafupi kuti mumve.+ Inu mitundu ya anthu,+ mvetserani. Dziko lapansi ndi zonse zimene zili mmenemo zimvetsere.+ Nthaka ya padziko lapansi+ ndi zonse zimene zili pamenepo zimve.+ Yeremiya 6:19 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 19 Tamverani, inu okhala padziko lapansi! Ine ndikubweretsa tsoka pa anthu awa+ chifukwa cha maganizo awo,+ pakuti sanamvere mawu anga ndipo anapitirizabe kukana chilamulo changa.”+ Mika 1:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 “Tamverani anthu nonsenu. Mvetsera mwatcheru iwe dziko lapansi ndi anthu onse okhala mwa iwe.+ Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa akhale mboni yokutsutsani pa zimene mukuchita.+ Yehova akutsutseni ali m’kachisi wake woyera.+
26 ndikutenga kumwamba ndi dziko lapansi+ lero monga mboni zokutsutsani, kuti mudzafafanizidwa mwamsanga m’dziko limene mukupita kukalitenga mutawoloka Yorodano. Simudzatalikitsa masiku anu m’dzikomo chifukwa mudzawonongedwa ndithu.+
2 Imvani+ kumwamba inu, ndipo tchera khutu iwe dziko lapansi, chifukwa Yehova wanena kuti: “Ndalera ana ndi kuwakulitsa,+ koma iwo andipandukira.+
34 Mitundu inu, bwerani pafupi kuti mumve.+ Inu mitundu ya anthu,+ mvetserani. Dziko lapansi ndi zonse zimene zili mmenemo zimvetsere.+ Nthaka ya padziko lapansi+ ndi zonse zimene zili pamenepo zimve.+
19 Tamverani, inu okhala padziko lapansi! Ine ndikubweretsa tsoka pa anthu awa+ chifukwa cha maganizo awo,+ pakuti sanamvere mawu anga ndipo anapitirizabe kukana chilamulo changa.”+
2 “Tamverani anthu nonsenu. Mvetsera mwatcheru iwe dziko lapansi ndi anthu onse okhala mwa iwe.+ Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa akhale mboni yokutsutsani pa zimene mukuchita.+ Yehova akutsutseni ali m’kachisi wake woyera.+