Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 6:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Bisalani, inu ana a Benjamini, thawani pakati pa Yerusalemu. Ku Tekowa+ imbani lipenga la nyanga ya nkhosa.+ Ku Beti-hakeremu+ kwezani moto wa chizindikiro, chifukwa chiwonongeko chachikulu, tsoka, lasuzumira kuchokera kumpoto.+

  • Yeremiya 10:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Tamvetserani nkhani imene yamveka! Kugunda kwakukulu kukumveka kuchokera kudziko la kumpoto,+ ndipo kudzasandutsa mizinda ya Yuda kukhala mabwinja, malo obisalamo mimbulu.+

  • Yeremiya 47:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Yehova anati:

      “Taonani! Madzi akubwera+ kuchokera kumpoto+ ndipo madzi ake ndi achigumula. Adzamiza dziko ndi zonse zokhala mmenemo.+ Adzamizanso mzinda ndi zonse zokhala mmenemo. Amuna adzalira mokuwa, ndipo aliyense wokhala m’dzikolo adzalira mofuula.+

  • Yeremiya 50:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Inetu ndikuutsira Babulo mpingo wa mitundu yamphamvu ndi kubweretsa mitunduyo kuchokera kudziko la kumpoto.+ Mitunduyo idzamuukira+ ndi kulanda dziko lake.+ Mauta awo ndi ofanana ndi mauta a munthu wamphamvu amene amapha ana ndipo mautawo sabwerera osachitapo kanthu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena