Levitiko 18:24 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 24 “‘Musadzidetse ndi chilichonse cha zinthu zimenezi, chifukwa mitundu imene ndikuichotsa pamaso panu yadzidetsa ndi zonse zimenezi.+ Numeri 35:33 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 33 “‘Musadetse dziko+ limene mukukhalamo, chifukwa magazi ndiwo amadetsa dziko. Ndipo dziko lodetsedwa ndi magazi silingayeretsedwe mwa njira ina, koma ndi magazi a munthu amene anakhetsa magaziyo.+ Deuteronomo 21:23 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 23 mtembo wake usakhale pamtengopo usiku wonse,+ koma uzionetsetsa kuti wamuika m’manda tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu.+ Usaipitse nthaka yako imene Yehova Mulungu wako akukupatsa monga cholowa.+ Salimo 78:58 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 58 Iwo anapitiriza kumukhumudwitsa ndi malo awo okwezeka,+Ndipo anamuchititsa nsanje ndi zifaniziro zawo zogoba.+ Salimo 106:38 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 38 Choncho anali kukhetsa magazi a anthu osalakwa,+Magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,Amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanani.+Ndipo dzikolo linaipa ndi magazi amene iwo anakhetsa.+ Yeremiya 16:18 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 18 Chotero ndisanawabwezeretse, ndidzawabwezera zolakwa zawo zonse+ ndi machimo awo onse chifukwa choipitsa dziko langa.+ Anadzaza cholowa changa ndi mitembo ya zinthu zawo zochititsa mseru ndiponso zinthu zawo zonyansazo.’”+ Ezekieli 36:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 “Iwe mwana wa munthu, pamene a nyumba ya Isiraeli anali kukhala m’dziko lawo, anali kudetsa dzikolo ndi njira zawo komanso zochita zawo.+ Pamaso panga, njira zawo zakhala ngati zonyansa za mkazi amene akusamba.+
24 “‘Musadzidetse ndi chilichonse cha zinthu zimenezi, chifukwa mitundu imene ndikuichotsa pamaso panu yadzidetsa ndi zonse zimenezi.+
33 “‘Musadetse dziko+ limene mukukhalamo, chifukwa magazi ndiwo amadetsa dziko. Ndipo dziko lodetsedwa ndi magazi silingayeretsedwe mwa njira ina, koma ndi magazi a munthu amene anakhetsa magaziyo.+
23 mtembo wake usakhale pamtengopo usiku wonse,+ koma uzionetsetsa kuti wamuika m’manda tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu.+ Usaipitse nthaka yako imene Yehova Mulungu wako akukupatsa monga cholowa.+
58 Iwo anapitiriza kumukhumudwitsa ndi malo awo okwezeka,+Ndipo anamuchititsa nsanje ndi zifaniziro zawo zogoba.+
38 Choncho anali kukhetsa magazi a anthu osalakwa,+Magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,Amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanani.+Ndipo dzikolo linaipa ndi magazi amene iwo anakhetsa.+
18 Chotero ndisanawabwezeretse, ndidzawabwezera zolakwa zawo zonse+ ndi machimo awo onse chifukwa choipitsa dziko langa.+ Anadzaza cholowa changa ndi mitembo ya zinthu zawo zochititsa mseru ndiponso zinthu zawo zonyansazo.’”+
17 “Iwe mwana wa munthu, pamene a nyumba ya Isiraeli anali kukhala m’dziko lawo, anali kudetsa dzikolo ndi njira zawo komanso zochita zawo.+ Pamaso panga, njira zawo zakhala ngati zonyansa za mkazi amene akusamba.+