31 “‘Phokoso lidzamveka kumalekezero a dziko lapansi, pakuti Yehova akufuna kuimba mlandu mitundu ya anthu.+ Iye mwini adzalimbana ndi anthu onse powaweruza.+ Anthu oipa adzawapha ndi lupanga,’+ watero Yehova.
4Tamverani mawu a Yehova inu ana a Isiraeli. Yehova ali ndi mlandu ndi anthu okhala m’dzikoli,+ chifukwa m’dzikoli mulibe choonadi,+ kukoma mtima kosatha, ndiponso anthu a m’dzikoli amachita zinthu ngati kuti sadziwa Mulungu.+