Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 113:1-9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 113 Tamandani Ya, anthu inu!+

      Inu atumiki a Yehova, mutamandeni,+

      Tamandani dzina la Yehova.+

       2 Dzina la Yehova lidalitsike,+

      Kuyambira tsopano mpaka kalekale.+

       3 Kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera,+

      Dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.+

       4 Yehova wakwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.+

      Ulemerero wake uli pamwamba pa kumwamba.+

       5 Ndani angafanane ndi Yehova Mulungu wathu,+

      Amene amakhala pamwamba?+

       6 Iye amatsika m’munsi kuti aone kumwamba ndi dziko lapansi.+

       7 Amadzutsa munthu wonyozeka kumuchotsa m’fumbi.+

      Amakweza munthu wosauka kumuchotsa padzala,+

       8 Kuti amukhazike pamodzi ndi anthu olemekezeka,+

      Pamodzi ndi anthu olemekezeka pakati pa anthu a Mulungu.+

       9 Akuchititsa mkazi wosabereka kukhala m’nyumba+

      Monga mayi wosangalala wa ana aamuna.+

      Tamandani Ya, anthu inu!+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena