13 Koma kalonga+ wa ufumu wa Perisiya+ ananditsekereza+ kwa masiku 21, ndipo Mikayeli,+ mmodzi mwa akalonga aakulu+ anabwera kudzandithandiza, ndipo pa nthawi imeneyo ndinakhalabe pafupi ndi mafumu a Perisiya.+
4 Ndithu, Mulungu sanalekerere angelo+ amene anachimwa aja osawapatsa chilango, koma mwa kuwaponya mu Tatalasi,*+ anawaika m’maenje a mdima wandiweyani powasungira chiweruzo.+