Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 17
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Nsembe zizikhala zopanda chilema (1)

      • Zoyenera kuchita ndi ampatuko (2-7)

      • Milandu yovuta kuweruza (8-13)

      • Malangizo oti mafumu azidzatsatira (14-20)

        • Mfumu izikopera buku la Chilamulo (18)

Deuteronomo 17:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 22:20; De 15:21; Mki 1:8

Deuteronomo 17:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:23; 13:6-9

Deuteronomo 17:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:19
  • +De 13:12-15

Deuteronomo 17:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yoh 7:51

Deuteronomo 17:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 13:6, 10

Deuteronomo 17:6

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “aziphedwa pakamwa pa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 18:16; Yoh 8:17; 1Ti 5:19; Ahe 10:28
  • +Nu 35:30; De 19:15

Deuteronomo 17:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 13:5; 1Ak 5:13

Deuteronomo 17:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 35:11
  • +De 12:5; 1Mf 3:16, 28; Sl 122:2, 5

Deuteronomo 17:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Sa 7:15, 16
  • +De 19:17; 21:5

Deuteronomo 17:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mki 2:7
  • +De 5:32; 12:32

Deuteronomo 17:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 11:2; Ahe 10:28
  • +De 13:5; 1Ak 5:13

Deuteronomo 17:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 13:11; 19:20

Deuteronomo 17:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Sa 8:5, 20; 10:19

Deuteronomo 17:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Sa 9:17; 10:24; 16:12, 13

Deuteronomo 17:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 20:1; 2Sa 8:4; Sl 20:7; Miy 21:31
  • +Yes 31:1

Deuteronomo 17:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 11:1-3; Ne 13:26
  • +Yob 31:24, 28; 1Ti 6:9

Deuteronomo 17:18

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “mpukutu umene.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 31:9, 26; 2Mf 22:8

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    3/15/2007, tsa. 20

    5/1/1995, ptsa. 12-13

Deuteronomo 17:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Mb 34:18
  • +Sl 1:2; 119:97

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/2002, ptsa. 12-17

    10/1/2000, tsa. 8

    5/1/1995, ptsa. 12-13

Deuteronomo 17:20

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    5/1/1995, ptsa. 12-13

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 17:1Le 22:20; De 15:21; Mki 1:8
Deut. 17:2De 4:23; 13:6-9
Deut. 17:3De 4:19
Deut. 17:3De 13:12-15
Deut. 17:4Yoh 7:51
Deut. 17:5De 13:6, 10
Deut. 17:6Mt 18:16; Yoh 8:17; 1Ti 5:19; Ahe 10:28
Deut. 17:6Nu 35:30; De 19:15
Deut. 17:7De 13:5; 1Ak 5:13
Deut. 17:8Nu 35:11
Deut. 17:8De 12:5; 1Mf 3:16, 28; Sl 122:2, 5
Deut. 17:91Sa 7:15, 16
Deut. 17:9De 19:17; 21:5
Deut. 17:11Mki 2:7
Deut. 17:11De 5:32; 12:32
Deut. 17:12Miy 11:2; Ahe 10:28
Deut. 17:12De 13:5; 1Ak 5:13
Deut. 17:13De 13:11; 19:20
Deut. 17:141Sa 8:5, 20; 10:19
Deut. 17:151Sa 9:17; 10:24; 16:12, 13
Deut. 17:16De 20:1; 2Sa 8:4; Sl 20:7; Miy 21:31
Deut. 17:16Yes 31:1
Deut. 17:171Mf 11:1-3; Ne 13:26
Deut. 17:17Yob 31:24, 28; 1Ti 6:9
Deut. 17:18De 31:9, 26; 2Mf 22:8
Deut. 17:192Mb 34:18
Deut. 17:19Sl 1:2; 119:97
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 17:1-20

Deuteronomo

17 “Musamapereke kwa Yehova Mulungu wanu nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena vuto lililonse, chifukwa idzakhala yonyansa kwa Yehova Mulungu wanu.+

2 Ngati pakati panu papezeka mwamuna kapena mkazi amene akuchita zinthu zoipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu, mu umodzi mwa mizinda yanu imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndipo akuphwanya pangano la Mulungu,+ 3 moti wasochera ndipo amalambira milungu ina nʼkumaigwadira, kapena kugwadira dzuwa, mwezi kapena gulu lonse la zinthu zakuthambo,+ zomwe ine sindinakulamuleni,+ 4 ndiye munthu wina akakuuzani zimenezi kapena mwamva zimene zachitika, muzifufuza nkhaniyo mosamala. Mukatsimikizira kuti ndi zoonadi+ kuti chinthu choipachi chachitika mu Isiraeli, 5 muzitenga mwamuna kapena mkazi amene wachita chinthu choipayo nʼkupita naye kunja kwa mzinda, ndipo muzikamuponya miyala kuti afe.+ 6 Munthuyo aziphedwa ngati pali umboni wa* anthu awiri kapena atatu.+ Asaphedwe ngati munthu mmodzi yekha ndi amene wapereka umboni.+ 7 Dzanja la mbonizo lizikhala loyamba kumuponya miyala kuti afe, ndipo anthu ena onse azibwera pambuyo. Choncho muzichotsa woipayo pakati panu.+

8 Ngati mu umodzi mwa mizinda yanu muli mlandu wovuta kwambiri kuweruza kaya ndi mlandu wokhudza kukhetsa magazi,+ mlandu umene munthu wakasuma, mlandu wokhudza zachiwawa kapena mkangano, muzinyamuka nʼkupita kumalo amene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.+ 9 Muzipita kwa Alevi omwe ndi ansembe ndi kwa woweruza+ amene akutumikira mʼmasiku amenewo. Muziwafotokozera nkhaniyo ndipo iwo azikuuzani chigamulo.+ 10 Kenako muzichita mogwirizana ndi chigamulo chimene akuuzani kumalo amene Yehova adzasankhe. Muzionetsetsa kuti mukuchita zonse zimene akulangizani. 11 Muzichita mogwirizana ndi lamulo limene akusonyezani komanso chigamulo chimene akuuzani.+ Musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere pa chigamulo chimene akupatsani.+ 12 Munthu amene adzachite zinthu modzikuza posamvera wansembe amene akutumikira Yehova Mulungu wanu kapena woweruza, ayenera kufa.+ Muzichotsa woipayo mu Isiraeli.+ 13 Anthu onse adzamva zimenezo nʼkuchita mantha ndipo sadzachitanso zinthu modzikuza.+

14 Mukakalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani nʼkulitenga kukhala lanu ndipo mukukhalamo, ndiye inu nʼkunena kuti, ‘Tisankhe mfumu ngati mitundu ina yonse imene yatizungulira,’+ 15 mudzasankhe mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.+ Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Simukuloledwa kusankha mlendo amene si mʼbale wanu. 16 Koma iye asakhale ndi mahatchi ambiri+ kapena kuchititsa anthu kuti abwerere ku Iguputo kuti akatenge mahatchi ochuluka+ chifukwa Yehova anakuuzani kuti, ‘Musabwererenso kudzera njira iyi.’ 17 Asakhalenso ndi akazi ambiri kuti mtima wake usapatuke+ komanso asakhale ndi siliva ndi golide wambiri.+ 18 Akakhala pampando wachifumu, ayenera kukopera buku lakelake la Chilamulo ichi, kuchokera mʼbuku limene* Alevi omwe ndi ansembe amasunga.+

19 Buku limeneli azikhala nalo nthawi zonse ndipo aziliwerenga masiku onse a moyo wake,+ kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake ndi kusunga mawu onse a Chilamulo ichi, komanso kutsatira malangizo ake.+ 20 Akachita zimenezi sadzadzikweza pamaso pa abale ake, komanso sadzachoka pachilamulo nʼkupatukira kudzanja lamanja kapena lamanzere, kuti iyeyo ndi ana ake apitirize kukhala mafumu mu Isiraeli kwa nthawi yaitali.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena