Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 8
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Nyimbo ya Solomo

    • MSULAMI ALI KU YERUSALEMU (3:6–8:4)

    • MSULAMI WABWERERA KWAWO, WASONYEZA KUTI NDI WOKHULUPIRIKA (8:5-14)

        • Azichimwene ake a mtsikana (5a)

          • ‘Kodi ndi ndani amene wakoleka dzanja mʼkhosi mwa wachikondi wake?’

        • Mtsikana (5b-7)

          • “Mofanana ndi Manda, chikondi sichigonja” (6)

        • Azichimwene ake a mtsikana (8, 9)

          • “Akakhala khoma, . . . koma akakhala chitseko, . . .” (9)

        • Mtsikana (10-12)

          • “Ine ndine khoma” (10)

        • Mʼbusa (13)

          • ‘Ndikufuna ndimve mawu akoʼ

        • Mtsikana (14)

          • “Thamanga ngati insa”

Nyimbo ya Solomo 8:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:2

Nyimbo ya Solomo 8:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 3:4

Nyimbo ya Solomo 8:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:6

Nyimbo ya Solomo 8:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:7; 3:5

Nyimbo ya Solomo 8:6

Mawu a M'munsi

  • *

    Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

  • *

    “Ya” ndi chidule cha dzina lakuti Yehova.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yoh 15:13; Aef 5:25; Chv 12:11
  • +De 4:24; 1Yo 4:8

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    5/2023, tsa. 20

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 29

    5/15/2012, tsa. 4

    11/15/2006, tsa. 20

    11/15/1987, tsa. 25

Nyimbo ya Solomo 8:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “munthuyo.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Ak 13:8, 13
  • +Aro 8:38, 39

Nyimbo ya Solomo 8:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:6

Nyimbo ya Solomo 8:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Galamukani!,

    3/8/1992, tsa. 10

Nyimbo ya Solomo 8:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mla 2:4

Nyimbo ya Solomo 8:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 1:6; 6:11
  • +Nym 2:14

Nyimbo ya Solomo 8:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:9, 17

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 8:1Nym 1:2
Nyimbo 8:2Nym 3:4
Nyimbo 8:3Nym 2:6
Nyimbo 8:4Nym 2:7; 3:5
Nyimbo 8:6Yoh 15:13; Aef 5:25; Chv 12:11
Nyimbo 8:6De 4:24; 1Yo 4:8
Nyimbo 8:71Ak 13:8, 13
Nyimbo 8:7Aro 8:38, 39
Nyimbo 8:8Nym 1:6
Nyimbo 8:11Mla 2:4
Nyimbo 8:13Nym 1:6; 6:11
Nyimbo 8:13Nym 2:14
Nyimbo 8:14Nym 2:9, 17
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 8:1-14

Nyimbo ya Solomo

8 “Ndikulakalaka ukanakhala mchimwene wanga,

Amene anayamwa mabere a mayi anga.

Ndikanakupeza panja, ndikanakukisa,+

Ndipo palibe amene akanandinyoza.

 2 Bwenzi nditakutsogolera.

Ndikanakulowetsa mʼnyumba mwa mayi anga,+

Amene ankandiphunzitsa.

Ndikanakupatsa vinyo wothira zonunkhiritsa kuti umwe,

Komanso madzi a zipatso za makangaza zongofinya kumene.

 3 Dzanja lake lamanzere likanakhala pansi pa mutu wanga,

Ndipo dzanja lake lamanja likanandikumbatira.+

 4 Ndakulumbiritsani inu ana aakazi a ku Yerusalemu kuti:

Musayese kudzutsa chikondi mwa ine nthawi yake isanakwane.”+

 5 “Kodi ndi ndani amene akuchokera kuchipululuyu,

Atakoleka dzanja lake mʼkhosi mwa wachikondi wake?”

“Ine ndinakudzutsa pansi pa mtengo wa maapozi.

Pamenepo mʼpamene mayi ako anamva zowawa pokubereka.

Mayi amene anakubereka anamva zowawa ali pamenepo.

 6 Undiike pamtima pako ngati chidindo,

Ndiponso undiike ngati chidindo padzanja lako,

Chifukwa mofanana ndi Manda,* chikondi sichigonja,+

Ndipo chimafuna kudzipereka ndi mtima wonse.

Chikondi chimenechi chili ngati malawi a moto. Chikondicho ndi lawi la Ya.*+

 7 Madzi osefukira sangazimitse chikondi,+

Ndipo mitsinje singachikokolole.+

Ngati munthu atapereka chuma chonse chamʼnyumba mwake kusinthanitsa ndi chikondi,

Anthu anganyoze zinthuzo.”*

 8 “Tili ndi mchemwali wathu wamngʼono+

Ndipo alibe mabere.

Kodi tidzamuchitire chiyani mchemwali wathuyu

Pa tsiku limene adzafunsiridwe ukwati?”

 9 “Akakhala khoma,

Timʼmangira kampanda kasiliva pamwamba pake,

Koma akakhala chitseko,

Timʼkhomerera ndi thabwa la mkungudza.”

10 “Ine ndine khoma,

Ndipo mabere anga ali ngati nsanja.

Choncho mʼmaso mwa wokondedwa wanga ndakhala

Ngati mkazi amene wapeza mtendere.

11 Solomo anali ndi munda wa mpesa+ ku Baala-hamoni.

Munda wa mpesawo anaupereka kwa anthu oti aziusamalira.

Ndipo munthu aliyense ankabweretsa ndalama zasiliva zokwana 1,000 zolipirira zipatso za mundawo.

12 Ndili ndi munda wanga wa mpesa umene ndingathe kuchita nawo chilichonse chimene ndikufuna.

Ndalama 1,000 zasilivazo ndi zanu inu a Solomo,

Ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za anthu amene amasamalira zipatso za mundawo.”

13 “Iwe amene umakhala mʼminda,+

Anzanga akufuna amve mawu ako.

Inenso ndikufuna ndimve mawu ako.”+

14 “Fulumira wachikondi wanga,

Thamanga ngati insa+

Kapena ngati mphoyo yaingʼono

Pamapiri amaluwa onunkhira.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena