Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 2
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Nyimbo ya Solomo

    • MSULAMI ALI MUMSASA WA MFUMU SOLOMO (1:1–3:5)

Nyimbo ya Solomo 2:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:16

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, ptsa. 31-32

    11/15/1987, tsa. 24

Nyimbo ya Solomo 2:2

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, ptsa. 31-32

    11/15/1987, tsa. 24

Nyimbo ya Solomo 2:3

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/1987, tsa. 24

Nyimbo ya Solomo 2:4

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “kunyumba ya vinyo.”

Nyimbo ya Solomo 2:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Sa 30:11, 12

Nyimbo ya Solomo 2:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 8:3

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2006, tsa. 18

Nyimbo ya Solomo 2:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Sa 2:18
  • +Nym 3:5; 8:4

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 31

    11/15/2006, ptsa. 18-19

    11/15/1987, ptsa. 24-25

Nyimbo ya Solomo 2:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 2:17; 8:14

Nyimbo ya Solomo 2:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 32

    Galamukani!,

    4/8/1994, ptsa. 24-25

Nyimbo ya Solomo 2:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 6:11
  • +Yes 18:5; Yoh 15:2
  • +Yer 8:7

Nyimbo ya Solomo 2:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 28:4; Nah 3:12

Nyimbo ya Solomo 2:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 5:2; Yer 48:28
  • +Nym 8:13
  • +Nym 1:5; 6:10

Nyimbo ya Solomo 2:15

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Galamukani!,

    4/8/1994, ptsa. 24-25

Nyimbo ya Solomo 2:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nym 7:10
  • +Nym 1:7
  • +Nym 2:1; 6:3

Nyimbo ya Solomo 2:17

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “mapiri amipata.” Kapena kuti, “mapiri a Belita.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Sa 2:18
  • +Nym 2:9; 8:14

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 2:1Nym 2:16
Nyimbo 2:51Sa 30:11, 12
Nyimbo 2:6Nym 8:3
Nyimbo 2:72Sa 2:18
Nyimbo 2:7Nym 3:5; 8:4
Nyimbo 2:9Nym 2:17; 8:14
Nyimbo 2:12Nym 6:11
Nyimbo 2:12Yes 18:5; Yoh 15:2
Nyimbo 2:12Yer 8:7
Nyimbo 2:13Yes 28:4; Nah 3:12
Nyimbo 2:14Nym 5:2; Yer 48:28
Nyimbo 2:14Nym 8:13
Nyimbo 2:14Nym 1:5; 6:10
Nyimbo 2:16Nym 7:10
Nyimbo 2:16Nym 1:7
Nyimbo 2:16Nym 2:1; 6:3
Nyimbo 2:172Sa 2:18
Nyimbo 2:17Nym 2:9; 8:14
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 2:1-17

Nyimbo ya Solomo

2 “Ine ndine duwa wamba lamʼchigwa chamʼmphepete mwa nyanja,

Ndine duwa chabe lamʼchigwa.”+

 2 “Mofanana ndi duwa limene lili pakati pa minga,

Ndi mmene alili wokondedwa wanga pakati pa ana aakazi.”

 3 “Mofanana ndi mtengo wa maapozi pakati pa mitengo yamʼnkhalango,

Ndi mmene alili wachikondi wanga pakati pa ana aamuna.

Ndikulakalaka kwambiri nditakhala pansi pamthunzi wa wokondedwa wanga.

Ndipo chipatso chake ndi chotsekemera.

 4 Iye anandipititsa kunyumba ya phwando,*

Ndipo chikondi chake kwa ine chinali ngati mbendera yozikidwa pambali panga.

 5 Ndipatseni mphesa zouma zoumba pamodzi+ kuti zinditsitsimule.

Ndipatseni maapozi kuti ndipeze mphamvu,

Chifukwa chikondi chikundidwalitsa.

 6 Dzanja lake lamanzere lili pansi pa mutu wanga,

Ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.+

 7 Ndakulumbiritsani inu ana aakazi a ku Yerusalemu,

Pali insa+ ndiponso pali mphoyo zakutchire kuti:

Musayese kudzutsa chikondi mwa ine nthawi yake isanakwane.+

 8 Ndikumva wachikondi wanga akubwera.

Taonani! Uyo akubwera apoyo,

Akukwera mapiri ndipo akudumpha zitunda.

 9 Wachikondi wanga ali ngati insa komanso mphoyo yaingʼono.+

Taonani! Iye waima kuseri kwa khoma la nyumba yathu.

Akuyangʼana mʼmawindo,

Akusuzumira pazotchingira mʼmawindo.

10 Wachikondi wanga wandiuza kuti:

‘Nyamuka wokondedwa wanga,

Ndiwe wokongola kwa ine, tiye tizipita.

11 Taona! Nyengo yamvula yadutsa.

Mvula yatha ndipo yapita.

12 Maluwa ayamba kuoneka mʼdziko,+

Nthawi yodulira mpesa yakwana,+

Ndipo mʼdziko lathu mukumveka kuimba kwa njiwa.+

13 Nkhuyu zoyambirira+ zapsa mumtengo wa mkuyu.

Mpesa wachita maluwa ndipo ukununkhira.

Nyamuka bwera kuno,

Wokondedwa wanga wokongola, tiye tizipita.

14 Iwe njiwa yanga, amene uli mʼmalo obisika apathanthwe,+

Amene uli mʼmingʼalu yamʼmalo otsetsereka,

Ndikufuna ndikuone komanso kumva mawu ako,+

Chifukwa mawu ako ndi osangalatsa ndipo iweyo ndiwe wokongola.’”+

15 “Tigwirireni nkhandwe,

Nkhandwe zingʼonozingʼono zimene zikuwononga minda ya mpesa,

Chifukwa minda yathu ya mpesa yachita maluwa.”

16 “Wachikondi wanga ndi wanga, ndipo ine ndine wake.+

Iye akudyetsa ziweto msipu+ umene uli pakati pa maluwa.+

17 Mpaka kunja kutayamba kuwomba kamphepo kayaziyazi ndiponso mpaka mithunzi itachoka,

Bwerera mwamsanga iwe wachikondi wanga,

Kwera mapiri amene akutilekanitsa,* ngati insa+ komanso ngati mphoyo yaingʼono.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena