Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • bi12 tsamba 1972-1983
  • Nkhani za M’baibulo Zokambirana

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nkhani za M’baibulo Zokambirana
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Timitu
  • 1. Aneneri Onyenga
  • 2. Aramagedo
  • 3. Baibulo
  • 4. Chikumbutso, Misa
  • 5. Chilengedwe
  • 6. Chipembedzo
  • 7. Chipulumutso
  • 8. Dipo
  • 9. Dziko Lapansi
  • 10. Imfa
  • 11. Kubweranso kwa Khristu
  • 13. Kuchitira Umboni
  • 14. Kulambira Makolo Akale
  • 15. Kulambira Mariya
  • 16. Kumwamba
  • 17. Kuphatikiza Zipembedzo
  • 18. Kutsutsidwa, Kuzunzidwa
  • 19. Kuuka kwa Akufa
  • 20. Kuwerengera Nthawi
  • 21. Magazi
  • 22. Maholide, Masiku a Kubadwa
  • 23. Masiku Otsiriza
  • 24. Mboni za Yehova
  • 25. Mdyerekezi, Ziwanda
  • 26. Moto
  • 27. Moyo
  • 28. Mtanda
  • 29. Mtumiki
  • 30. Mzimu, Kukhulupirira Mizimu
  • 31. Pemphero
  • 32. Sabata
  • 34. Tchimo
  • 35. Ubatizo
  • 37. Ukwati
  • 38. Utatu
  • 39. Yehova, Mulungu
  • 40. Yesu
  • 41. Zifaniziro
  • 42. Zoipa, Mavuto a m’Dziko
  • 43. Zolembedweratu
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nkhani za M’baibulo Zokambirana

Nkhani za M’baibulo Zokambirana

1. Aneneri Onyenga

A. Ananeneratu za aneneri onyenga, analiko m’masiku a atumwi

Njira yodziwira aneneri onyenga. De 18:20-22; Lu 6:26

Ananeneratu za iwo, amadziwika ndi zipatso zawo. Mt 24:23-26; 7:15-23

2. Aramagedo

A. Nkhondo ya Mulungu yothetsa zoipa zonse

Mitundu idzasonkhanitsidwa pa Aramagedo. Chv 16:14, 16

Mulungu adzamenya nkhondoyo, pogwiritsa ntchito Mwana wake ndi angelo. 2At 1:6-9; Chv 19:11-16

Mmene tingadzapulumukire. Zef 2:2, 3; Chv 7:14

B. Sikulephera kwa chikondi cha Mulungu

Dziko laipa kwambiri. 2Ti 3:1-5

Mulungu wakhala woleza mtima, koma ayenera kuchitapo kanthu chifukwa cha chilungamo. 2Pe 3:9, 15; Lu 18:7, 8

Oipa ayenera kuchoka kuti olungama asangalale. Miy 21:18; Chv 11:18

3. Baibulo

A. Mawu a Mulungu ndi ouziridwa

Anthu anatsogoleredwa ndi mzimu wa Mulungu kuti alembe. 2Pe 1:20, 21

Muli ulosi: Da 8:5, 6, 20-22; Lu 21:5, 6, 20-22; Yes 45:1-4

Baibulo lonse ndi louziridwa ndipo n’lopindulitsa. 2Ti 3:16, 17; Aro 15:4

B. Limapereka malangizo othandiza m’masiku athu ano

Kunyalanyaza mfundo za m’Baibulo n’kotayitsa moyo. Aro 1:28-32

Nzeru za anthu sizingalowe m’malo mwake. 1Ak 1:21, 25; 1Ti 6:20

N’chitetezo kwa mdani wamphamvu koposa. Aef 6:11, 12, 17

Limatsogolera anthu m’njira yoyenera. Sl 119:105; 2Pe 1:19; Miy 3:5, 6

C. Linalembedwera anthu a mitundu yonse ndi a mafuko onse

Baibulo linayamba kulembedwa kumayiko a Kum’mawa. Eks 17:14; 24:12, 16; 34:27

Mphatso ya Mulungu imeneyi si ya Azungu okha. Aro 10:11-13; Aga 3:28

Mulungu amalandira anthu, kaya akhale otani. Mac 10:34, 35; Aro 5:18; Chv 7:9, 10

4. Chikumbutso, Misa

A. Kuchita chikumbutso cha Chakudya Chamadzulo cha Ambuye

Kumachitika kamodzi pa chaka, pa deti la Pasika. Lu 22:1, 17-20; Eks 12:14

Ndi kukumbukira imfa ya Khristu yopereka nsembe. 1Ak 11:26; Mt 26:28

Amene ali ndi chiyembekezo chopita kumwamba amadya mkate ndi kumwa vinyo. Lu 22:29, 30; 12:32, 37

Mmene munthu amadziwira kuti ali ndi chiyembekezo chimenecho. Aro 8:15-17

B. Misa si ya m’Malemba

Kuti machimo akhululukidwe, pamafunika pakhetsedwe magazi. Ahe 9:22

Khristu ndiye Mkhalapakati yekhayo wa pangano latsopano. 1Ti 2:5, 6; Yoh 14:6

Khristu ali kumwamba, satsitsidwa pansi ndi wansembe. Mac 3:20, 21

Kubwereza nsembe ya Khristu n’kosafunikira. Ahe 9:24-26; 10:11-14

5. Chilengedwe

A. Chimagwirizana ndi sayansi yokhala ndi umboni wodalirika, chimatsutsa zoti zamoyo zinachita kusandulika

Sayansi imagwirizana ndi ndondomeko ya kulengedwa kwa zinthu. Ge 1:11, 12, 21, 24, 25

Lamulo la Mulungu lokhudza “mitundu” ya zolengedwa ndi loona. Ge 1:11, 12; Yak 3:12

B. Masiku olenga zinthu sanali masiku a maola 24

“Tsiku” lingatanthauze nthawi ya masiku ambiri. Ge 2:4

Kwa Mulungu, tsiku lingakhale nthawi yaitali. Sl 90:4; 2Pe 3:8

6. Chipembedzo

A. Chipembedzo choona n’chimodzi chokha

Chiyembekezo chimodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi. Aef 4:5, 13

Chinapatsidwa ntchito yophunzitsa anthu kuti akhale ophunzira. Mt 28:19; Mac 8:12; 14:21

Chimadziwika ndi zipatso zake. Mt 7:19, 20; Lu 6:43, 44; Yoh 15:8

Chikondi, anthu ake amalankhula zofanana. Yoh 13:35; 1Ak 1:10; 1Yoh 4:20

B. Sikulakwa kutsutsa ziphunzitso zonama

Yesu anatsutsa ziphunzitso zonama. Mt 23:15, 23, 24; 15:4-9

Anatero kuti ateteze amene anachititsidwa khungu. Mt 15:14

Choonadi chinawamasula kuti akhale ophunzira a Yesu. Yoh 8:31, 32

C. M’pofunika kusintha chipembedzo chako chikapezeka kuti n’cholakwika

Choonadi chimamasula, chimaonetsa kuti ambiri ndi olakwa. Yoh 8:31, 32

Aisiraeli ndi enanso, anasiya chipembedzo chawo chakale. Yos 24:15; 2Mf 5:17

Akhristu oyambirira anasintha maganizo awo. Aga 1:13, 14; Mac 3:17, 19

Paulo anasintha chipembedzo chake. Mac 26:4-6

Dziko lonse lanyengedwa, liyenera kusintha maganizo. Chv 12:9; Aro 12:2

D. Zooneka ngati “zabwino m’zipembedzo zonse” si zimene Mulungu amavomerezera chipembedzo

Mulungu ndiye amanena mmene tiyenera kumulambirira. Yoh 4:23, 24; Yak 1:27

Si zabwino ngati n’zosagwirizana ndi chifuniro cha Mulungu. Aro 10:2, 3

“Ntchito zabwino” zitha kukanidwa. Mt 7:21-23

Chimadziwika ndi zipatso zake. Mt 7:20

7. Chipulumutso

A. Chipulumutso chimachokera kwa Mulungu kudzera mu nsembe ya Yesu ya dipo

Moyo ndi mphatso ya Mulungu kudzera mwa Mwana wake. 1Yoh 4:9, 14; Aro 6:23

Chipulumutso n’chotheka kudzera mu nsembe ya Yesu yokha basi. Mac 4:12

Kulapa pomwalira sikukhala ndi ntchito za kulapa. Yak 2:14, 26

Tiyenera kuyesetsa mwamphamvu kuti tichipeze. Lu 13:23, 24; 1Ti 4:10

B. Mfundo yakuti “ukapulumutsidwa, wapulumutsidwa basi” si ya m’Malemba

Amene amalandira nawo mzimu woyera akhoza kugwa mwauzimu. Ahe 6:4, 6; 1Ak 9:27

Aisiraeli ambiri anawonongedwa ngakhale kuti anali atapulumutsidwa ku Iguputo. Yuda 5

Chipulumutso sichibwera kamodzi n’kamodzi. Afi 2:12; 3:12-14; Mt 10:22

Obwerera m’mbuyo amakhala oipa kwambiri kuposa poyamba. 2Pe 2:20, 21

C. Chiphunzitso chakuti “aliyense adzapulumuka” si cha m’Malemba

Ena sangathe kulapa. Ahe 6:4-6

Mulungu sakondwera ndi imfa ya oipa. Eze 33:11; 18:32

Koma chikondi sichilekerera zosalungama. Ahe 1:9

Oipa adzawonongedwa. Ahe 10:26-29; Chv 20:7-15

8. Dipo

A. Moyo wa Yesu pamene anali munthu unaperekedwa monga “dipo la onse”

Yesu anapereka moyo wake dipo. Mt 20:28

Magazi ake amtengo wapatali amafafaniza machimo. Ahe 9:14, 22

Nsembe imodzi ndi yokwanira mpaka kalekale. Aro 6:10; Ahe 9:26

Munthu ayenera kuchitapo kanthu kuti apindule nayo, ayenera kuvomereza nsembeyo. Yoh 3:16

B. Dipolo linali lofanana ndi zimene zinatayika

Adamu analengedwa wangwiro. De 32:4; Mla 7:29; Ge 1:31

Atachimwa, anakhala wopanda ungwiro ndipo anachititsanso kuti ana ake akhale opanda ungwiro. Aro 5:12, 18

Ana sakanatha kuchitapo kanthu, panafunikira wofanana ndendende ndi Adamu. Sl 49:7; De 19:21

Moyo wangwiro wa Yesu pamene anali munthu unaperekedwa kuti ukhale dipo. 1Ti 2:5, 6; 1Pe 1:18, 19

9. Dziko Lapansi

A. Cholinga cha Mulungu chokhudza dziko lapansi

Paradaiso anapangidwa padziko lapansi kuti anthu angwiro akhalemo. Ge 1:28; 2:8-15

Cholinga cha Mulungu chidzakwaniritsidwa. Yes 55:11; 46:10, 11

Dziko lidzadzaza ndi anthu angwiro amtendere. Sl 72:7; Yes 45:18; 9:6, 7

Ufumu udzabwezeretsa Paradaiso. Mt 6:9, 10; Chv 21:3-5

B. Silidzawonongedwa kapena kukhala lopanda anthu

Dziko lapansi lenilenili lidzakhalapo mpaka kalekale. Mla 1:4; Sl 104:5

Mu nthawi ya Nowa anthu ndiwo anawonongedwa, osati dziko lapansi. 2Pe 3:5-7; Ge 7:23

Chitsanzochi chikutipatsa chiyembekezo chakuti anthu apulumuka mu nthawi yathu ino. Mt 24:37-39

Oipa adzawonongedwa, “khamu lalikulu” lidzapulumuka. 2At 1:6-9; Chv 7:9, 14

10. Imfa

A. Chochititsa imfa

Pa chiyambi anthu anali angwiro, anali ndi chiyembekezo chokhala ndi moyo wosatha. Ge 1:28, 31

Kusamvera kunabweretsa chiweruzo cha imfa. Ge 2:16, 17; 3:17, 19

Uchimo ndi imfa zinafikanso kwa ana onse a Adamu. Aro 5:12

B. Mmene akufa alili

Akufa sazindikira kanthu, sadziwa chilichonse. Mla 9:5, 10; Sl 146:3, 4

Akufa ali m’tulo kuyembekezera kuukitsidwa. Yoh 11:11-14, 23-26; Mac 7:60

C. N’zosatheka kulankhula ndi akufa

Akufa sali ndi moyo limodzi ndi Mulungu monga mizimu. Sl 115:17; Yes 38:18

Tikuchenjezedwa kuti tisayese kulankhula ndi akufa. Yes 8:19; Le 19:31

Olankhula ndi mizimu, olosera za m’tsogolo, n’ngosavomerezedwa. De 18:10-12; Aga 5:19-21

11. Kubweranso kwa Khristu

A. Kubweranso kwake n’kosaoneka kwa anthu

Anauza ophunzira ake kuti dziko silidzamuonanso. Yoh 14:19

Ophunzira okha ndiwo anamuona akukwera kumwamba, chimodzimodzi pa kubweranso kwake. Mac 1:6, 10, 11

Ali kumwamba monga mzimu wosaoneka. 1Ti 6:14-16; Ahe 1:3

Abwerera monga mfumu yamphamvu ya Ufumu wakumwamba. Da 7:13, 14

B. Kudzadziwika ndi zochitika zooneka ndi maso

Ophunzira anapempha chizindikiro cha kukhalapo kwake. Mt 24:3

Akhristu “amaona” kukhalapo kwake mwa kuzindikira zochitika. Aef 1:18

Zochitika zambiri zikusonyeza umboni wa kukhalapo kwake. Lu 21:10, 11

Adani “adzaona” chiwonongeko chitawagwera. Chv 1:7

12. Kuchiritsa, Malilime

A. Kuchiritsidwa mwauzimu kumapindulitsa kwamuyaya

Matenda auzimu amawononga. Yes 1:4-6; 6:10; Ho 4:6

Kuchiritsa kwauzimu ndiko ntchito yaikulu imene tapatsidwa. Yoh 6:63; Lu 4:18

Kumachotsa machimo, kumapereka chimwemwe ndi moyo. Yak 5:19, 20; Chv 7:14-17

B. Mu Ufumu wa Mulungu anthu adzachiritsidwa ndipo sadzadwalanso

Yesu anachiritsa matenda, analalikira za madalitso a Ufumu. Mt 4:23

Ufumu wolonjezedwawo ndiwo njira yokhayo yochiritsira anthu kuti asadzadwalenso. Mt 6:10; Yes 9:7

Ngakhale imfa idzathetsedwa. 1Ak 15:25, 26; Chv 21:4; 20:14

C. Kuchiritsa kwamasiku ano kulibe umboni wakuti Mulungu amakuvomereza

Ophunzira sanali kudzichiritsa okha mozizwitsa. 2Ak 12:7-9; 1Ti 5:23

Mphatso zozizwitsa zinapita ndi masiku a atumwi. 1Ak 13:8-11

Kuchiritsa si umboni wotsimikizira kuti munthu akuvomerezedwa ndi Mulungu. Mt 7:22, 23; 2At 2:9-11

D. Kulankhula malilime kunali dongosolo lakanthawi chabe

Kunali chizindikiro, anthuwo anayenera kuyesetsa kupeza mphatso zina zazikulu. 1Ak 14:22; 12:30, 31

Ananeneratu kuti mphatso zozizwitsa za mzimu zidzatha. 1Ak 13:8-10

Kuchita zinthu zodabwitsa si umboni wotsimikizira kuti munthu akuvomerezedwa ndi Mulungu. Mt 7:22, 23; 24:24

13. Kuchitira Umboni

A. Akhristu onse ayenera kuchitira umboni, kuuza ena uthenga wabwino

Ayenera kuvomereza Yesu pamaso pa anthu kuti iwonso avomerezedwe. Mt 10:32

Ayenera kuchita zimene Mawu amanena, posonyeza chikhulupiriro. Yak 1:22-24; 2:24

Atsopano nawonso ayenera kukhala aphunzitsi. Mt 28:19, 20

Kulengeza pamaso pa anthu kumabweretsa chipulumutso. Aro 10:10

B. Kufunika kwa kufikira anthu mobwerezabwereza, kupitirizabe kulalikira

Chenjezo la mapeto liyenera kuperekedwa. Mt 24:14

Yeremiya analengeza kwa zaka zambiri mapeto a Yerusalemu. Yer 25:3

Mofanana ndi Akhristu oyambirira, sitingaleke. Mac 4:18-20; 5:28, 29

C. Tiyenera kuchitira umboni kuti tisakhale ndi mlandu wa magazi

Tiyenera kuchenjeza za mapeto amene akuyandikira. Eze 33:7; Mt 24:14

Kulephera kutero kumabweretsa mlandu wa magazi. Eze 33:8, 9; 3:18, 19

Paulo analibe mlandu wa magazi, analankhula choonadi chonse. Mac 20:26, 27; 1Ak 9:16

Kumapulumutsa wochitira umboniyo ndi womvetserayo. 1Ti 4:16; 1Ak 9:22

14. Kulambira Makolo Akale

A. Kulambira makolo akale n’kosathandiza

Makolo akale n’ngakufa, sadziwa kalikonse. Mla 9:5, 10

Makolo oyambirira ndi osayenera kuwalambira. Aro 5:12, 14; 1Ti 2:14

Mulungu amaletsa kulambira koteroko. Eks 34:14; Mt 4:10

B. Anthu angalemekezedwe, koma Mulungu yekha ndiye ayenera kulambiridwa

Achinyamata ayenera kulemekeza achikulire. 1Ti 5:1, 2, 17; Aef 6:1-3

Koma Mulungu yekha ndiye woyenera kumulambira. Mac 10:25, 26; Chv 22:8, 9

15. Kulambira Mariya

A. Mariya anali amayi a Yesu, osati “amayi a Mulungu”

Mulungu alibe chiyambi. Sl 90:2; 1Ti 1:17

Mariya anali amayi a Mwana wa Mulungu, pamene anali padziko lapansi. Lu 1:35

B. Mariya sanali “namwali moyo wake wonse”

Anakwatiwa ndi Yosefe. Mt 1:19, 20, 24, 25

Anakhalanso ndi ana ena kuwonjezera pa Yesu. Mt 13:55, 56; Lu 8:19-21

Pa nthawiyo iwo sanali ‘abale ake auzimu.’ Yoh 7:3, 5

16. Kumwamba

A. Anthu 144,000 okha ndiwo adzapite kumwamba

N’chiwerengero chochepa chabe, adzakhala mafumu limodzi ndi Khristu. Chv 5:9, 10; 20:4

Yesu anali kalambulabwalo, enanso anasankhidwa kuyambira nthawiyo. Akl 1:18; 1Pe 2:21

Anthu ena ambiri adzakhala padziko lapansi. Sl 72:8; Chv 21:3, 4

A 144,000 ali ndi udindo wapadera, palibenso ena ali nawo. Chv 14:1, 3; 7:4, 9

17. Kuphatikiza Zipembedzo

A. Kuphatikiza zipembedzo si kovomerezeka ndi Mulungu

Pali njira imodzi yokha, yopanikiza, oipeza ndi owerengeka. Aef 4:4-6; Mt 7:13, 14

Timachenjezedwa kuti ziphunzitso zonama zingatiipitse. Mt 16:6, 12; Aga 5:9

Tikulamulidwa kukhala olekana ndi enawo. 2Ti 3:5; 2Ak 6:14-17; Chv 18:4

B. Mfundo yakuti muli “zabwino m’zipembedzo zonse” si yoona

Ena ndi odzipereka koma mosagwirizana ndi Mulungu. Aro 10:2, 3

Choipa chimawononga zimene zikanakhala zabwino. 1Ak 5:6; Mt 7:15-17

Aphunzitsi onyenga ndi ophetsa. 2Pe 2:1; Mt 12:30; 15:14

Kulambira koyera kumafuna kuti munthu akhale wodzipereka ndi mtima wonse. De 6:5, 14, 15

18. Kutsutsidwa, Kuzunzidwa

A. Chifukwa chimene Akhristu amatsutsidwira

Yesu anadedwa, ananeneratu kuti Akhristu adzatsutsidwa. Yoh 15:18-20; Mt 10:22

Kutsatira mfundo zoyenera kumatsutsa dziko. 1Pe 4:1, 4, 12, 13

Satana, mulungu wa nthawi ino, amatsutsa Ufumu. 2Ak 4:4; 1Pe 5:8

Mkhristu saopa, Mulungu amathandiza. Aro 8:38, 39; Yak 4:8

B. Mkazi asalole kuti mwamuna wake amulekanitse ndi Mulungu

Akuchenjezedwa kuti anthu ena angauze mwamuna wake zolakwika. Mt 10:34-38; Mac 28:22

Mkazi adalire Mulungu ndi Khristu. Yoh 6:68; 17:3

Kukhulupirika kwake kungapulumutsenso mwamuna wake. 1Ak 7:16; 1Pe 3:1-6

Mwamuna ndiye mutu, koma asalamule pa nkhani ya kulambira. 1Ak 11:3; Mac 5:29

C. Mwamuna asalole kuti mkazi wake amuletse kutumikira Mulungu

Akonde mkazi wake ndi banja lake, azifuna kuti iwo adzapeze moyo. 1Ak 7:16

Ali ndi udindo wosankhira banja lake zochita ndi kulipezera zosowa. 1Ak 11:3; 1Ti 5:8

Mulungu amakonda mwamuna wokhala ku mbali ya choonadi. Yak 1:12; 5:10, 11

Kugonjera potsutsidwa n’cholinga chakuti pakhale mtendere kumachititsa kuti Mulungu asakukonde. Ahe 10:38

Ayenera kutsogolera banja lake kuti lidzapeze moyo wosangalala m’dziko latsopano. Chv 21:3, 4

19. Kuuka kwa Akufa

A. Chiyembekezo chokhudza akufa

Onse amene ali m’manda adzaukitsidwa. Yoh 5:28, 29

Kuukitsidwa kwa Yesu kumatsimikizira zimenezi. 1Ak 15:20-22; Mac 17:31

Ochimwira mzimu sadzauka. Mt 12:31, 32

Okhulupirira akutsimikiziridwa kuti adzauka. Yoh 11:25

B. Kuukitsidwira ku moyo wakumwamba kapena padziko lapansi

Onse amafa mwa Adamu, amalandira moyo mwa Yesu. 1Ak 15:20-22; Aro 5:19

Amaukitsidwa ndi matupi osiyanasiyana. 1Ak 15:40, 42, 44

Okhala ndi Yesu adzakhala ngati iyeyo. 1Ak 15:49; Afi 3:20, 21

Osakhala ndi udindo wolamulira adzakhala padziko lapansi. Chv 20:4b, 5, 13; 21:3, 4

20. Kuwerengera Nthawi

A. Nthawi za Akunja zinatha mu 1914 (C.E.)

Mzere wa mafumu olamulira unadulidwa mu 607 B.C.E. Eze 21:25-27

Panayenera kudutsa “Nthawi 7” kuti ulamulirowo aubwezeretse. Da 4:32, 16, 17

Nthawi 7 = nthawi 3 1⁄2 × 2, kapena masiku 1,260 × 2.  Chv 12:6, 14; 11:2, 3

Tsiku limodzi kuimira chaka chimodzi. [Zikukwana zaka 2,520] Eze 4:6; Nu 14:34

Zakazo zinadzafika mpaka pa kukhazikitsidwa kwa Ufumu. Lu 21:24; Da 7:13, 14

21. Magazi

A. Kuikidwa magazi n’kusalemekeza kupatulika kwa magazi

Nowa anauzidwa kuti magazi ndi opatulika, ndiwo moyowo. Ge 9:4, 16

Pangano la Chilamulo linaletsa kudya magazi. Le 17:14; 7:26, 27

Akhristu anapatsidwanso lamulo limenelo. Mac 15:28, 29; 21:25

B. Kupulumutsa moyo si chifukwa chophwanyira lamulo la Mulungu

Kumvera kuposa nsembe. 1Sa 15:22; Mko 12:33

Kuika moyo wako patsogolo pa lamulo la Mulungu n’kophetsa. Mko 8:35, 36

22. Maholide, Masiku a Kubadwa

A. Akhristu oyambirira sanali kusunga masiku a kubadwa, Khirisimasi

Amene si olambira oona ndiwo anasunga masikuwo. Ge 40:20; Mt 14:6

Tsiku la imfa ya Yesu liyenera kukumbukiridwa. Lu 22:19, 20; 1Ak 11:25, 26

Kuchita maphwando a phokoso pa tsikulo n’kosayenera. Aro 13:13; Aga 5:21; 1Pe 4:3

23. Masiku Otsiriza

A. Kodi “mapeto a dziko” amatanthauzanji?

Kutha kwa nthawi ino. Mt 24:3; 2Pe 3:5-7; Mko 13:4

Si kutha kwa dziko lapansi, koma kwa nthawi yoipa ino. 1Yoh 2:17

Nthawi ya mapeto choyamba, kenako chiwonongeko. Mt 24:14

Kupulumuka kwa olungama, kenako dziko latsopano. 2Pe 2:9; Chv 7:14-17

B. Kufunika kokhala maso n’kumaona zizindikiro za masiku otsiriza

Zizindikiro zinaperekedwa ndi Mulungu kuti zititsogolere. 2Ti 3:1-5; 1At 5:1-4

Dziko silizindikira kuopsa kwake. 2Pe 3:3, 4, 7; Mt 24:39

Mulungu sakuchedwa, koma akupereka chenjezo. 2Pe 3:9

Mphoto ya kukhala maso, osamala. Lu 21:34-36

24. Mboni za Yehova

A. Chiyambi cha Mboni za Yehova

Yehova amadziwikitsa mboni zake. Yes 43:10-12; Yer 15:16

Mzera wa mboni zokhulupirika unayambira pa Abele. Ahe 11:4, 39; 12:1

Yesu anali mboni yokhulupirika ndi yoona. Yoh 18:37; Chv 1:5; 3:14

25. Mdyerekezi, Ziwanda

A. Mdyerekezi ndi munthu wauzimu

Si zoipa za mumtima wa munthu koma iye ndi munthu wauzimu. 2Ti 2:26

Mdyerekezi ndi munthu wauzimu monga alili angelo. Mt 4:1, 11; Yob 1:6

Anadzipanga yekha kukhala Mdyerekezi polakalaka zinthu zoipa. Yak 1:13-15

B. Mdyerekezi ndiye wolamulira wosaoneka wa dziko

Dziko likulamulidwa ndi iye monga mulungu wake. 2Ak 4:4; 1Yoh 5:19; Chv 12:9

Analoledwa kukhalapobe mpaka nkhani idzathetsedwe. Eks 9:16; Yoh 12:31

Adzaponyedwa m’phompho, kenako adzawonongedwa. Chv 20:2, 3, 10

C. Ziwanda ndi angelo opanduka

Zinagwirizana ndi Satana Chigumula chisanachitike. Ge 6:1, 2; 1Pe 3:19, 20

Zinatsitsidwa, sizilandiranso kuunika kulikonse. 2Pe 2:4; Yuda 6

Zimalimbana ndi Mulungu, zimapondereza anthu. Lu 8:27-29; Chv 16:13, 14

Zidzawonongedwa pamodzi ndi Satana. Mt 25:41; Lu 8:31; Chv 20:2, 3, 10

26. Moto

A. Moto ukuphiphiritsira chiwonongeko

Moto ukuphiphiritsira kuwonongedwa mwa kuphedwa. Mt 25:41, 46; 13:30

Anthu oipa osalapa adzawonongedweratu ngati mmene moto umawonongera. Ahe 10:26, 27

‘Kuzunzidwa’ kwa Satana m’moto ndiko imfa yosabwererako. Chv 20:10, 14, 15

B. Nkhani ya munthu wachuma ndi Lazaro si umboni wakuti anthu adzazunzidwa kwamuyaya

Motowo ndi wophiphiritsa monganso kukhala pachifuwa cha Abulahamu. Lu 16:22-24

Kuvomerezedwa ndi Abulahamu anakusiyanitsanso ndi mdima. Mt 8:11, 12

Kuwonongedwa kwa Babulo kumatchedwanso kuzunzidwa m’moto. Chv 18:8-10, 21

27. Moyo

A. Anthu omvera akutsimikiziridwa kuti adzapeza moyo wosatha

Mulungu, amene sanganame, analonjeza moyo. Tit 1:2; Yoh 10:27, 28

Okhulupirira akutsimikiziridwa kuti adzapeza moyo wamuyaya. Yoh 11:25, 26

Imfa idzawonongedwa. 1Ak 15:26; Chv 21:4; 20:14; Yes 25:8

B. Moyo wakumwamba ndi wa okhawo amene ali m’thupi la Khristu

Mulungu amasankha anthu amene iye wafuna. Mt 20:23; 1Ak 12:18

Anthu 144,000 okha osankhidwa padziko lapansi. Chv 14:1, 4; 7:2-4; 5:9, 10

Ngakhale Yohane M’batizi sadzakhala mu Ufumu wakumwamba. Mt 11:11

C. Moyo wa padziko lapansi unalonjezedwa kwa anthu osawerengeka, “nkhosa zina”

Ochepa chabe ndiwo adzakhale ndi Yesu kumwamba. Chv 14:1, 4; 7:2-4

“Nkhosa zina” si abale a Khristu. Yoh 10:16; Mt 25:32, 40

Ambiri akusonkhanitsidwa panopa kuti adzapulumuke padziko lapansi. Chv 7:9, 15-17

Ena adzaukitsidwa kuti akhale ndi moyo padziko lapansi. Chv 20:12; 21:4

28. Mtanda

A. Yesu anapachikidwa pamtengo wopherapo olakwa kuti anyozeke

Yesu anapachikidwa pamtengo wopherapo anthu olakwa. Mac 5:30; 10:39; Aga 3:13

Akhristu ayenera kunyamula mtengowo, kutanthauza kuti ayenera kunyozeka. Mt 10:38; Lu 9:23

B. Suyenera kulambiridwa

Kuonetsera mtengo umene Yesu anaferapo ndi mnyozo. Ahe 6:6; Mt 27:41, 42

Kugwiritsa ntchito mtanda polambira ndi kulambira mafano. Eks 20:4, 5; Yer 10:3-5

Yesu ndi mzimu, salinso pamtengo. 1Ti 3:16; 1Pe 3:18

29. Mtumiki

A. Akhristu onse ayenera kukhala atumiki

Yesu anali mtumiki wa Mulungu. Aro 15:8, 9; Mt 20:28

Akhristu amatsatira chitsanzo chake. 1Pe 2:21; 1Ak 11:1

Ayenera kulalikira kuti akwaniritse utumiki. 2Ti 4:2, 5; 1Ak 9:16

B. Zimene zimayeneretsa munthu kuti akhale mtumiki

Mzimu wa Mulungu ndiponso kudziwa Mawu ake. 2Ti 2:15; Yes 61:1-3

Kutsatira njira ya Khristu ya kulalikira. 1Pe 2:21; 2Ti 4:2, 5

Mulungu amaphunzitsa mwa mzimu ndi gulu lake. Yoh 14:26; 2Ak 3:1-3

30. Mzimu, Kukhulupirira Mizimu

A. Kodi mzimu woyera n’chiyani?

Ndi mphamvu yogwira ntchito ya Mulungu, si munthu ayi. Mac 2:2, 3, 33; Yoh 14:17

Anaugwiritsa ntchito polenga, pouzira Baibulo, ndi zina zotero. Ge 1:2; Eze 11:5

Umabala ndi kudzoza ziwalo za thupi la Khristu. Yoh 3:5-8; 2Ak 1:21, 22

Umapatsa mphamvu anthu a Mulungu ndi kuwatsogolera masiku ano. Aga 5:16, 18

B. Mphamvu imene imapangitsa zamoyo kukhala ndi moyo imatchedwa mzimu

Ndi mphamvu yopangitsa chamoyo kukhala moyo, imachirikizidwa ndi kupuma. Yak 2:26; Yob 27:3

Mulungu ndiye ali ndi ulamuliro pa mphamvu yochirikiza moyo imeneyi. Zek 12:1; Mla 8:8

Mphamvu yochirikiza moyo ya anthu, nyama, mwiniwake ndi Mulungu. Mla 3:19-21

Munthu akafa, ulamuliro pa mphamvu ya moyo umabwerera kwa Mulungu. Mla 12:7; Lu 23:46

C. Kukhulupirira mizimu kuyenera kupewedwa popeza ndi ntchito ya ziwanda

Mawu a Mulungu amaletsa. Yes 8:19, 20; Le 19:31; 20:6, 27

Kulosera ndiko kukhulupirira ziwanda, n’koletsedwa. Mac 16:16-18

Kumabweretsa chiwonongeko. Aga 5:19-21; Chv 21:8; 22:15

Kukhulupirira nyenyezi n’koletsedwa. De 18:10-12; Yer 10:2

31. Pemphero

A. Mapemphero amene Mulungu amamva

Mulungu amamvetsera mapemphero a anthu. Sl 145:18; 1Pe 3:12

Samvera mapemphero a osalungama kupatulapo akasintha njira yawo. Yes 1:15-17

Tiyenera kupemphera m’dzina la Yesu. Yoh 14:13, 14; 2Ak 1:20

Tiyenera kupemphera mogwirizana ndi chifuniro cha Mulungu. 1Yoh 5:14, 15

Chikhulupiriro n’chofunikira. Yak 1:6-8

B. Mapemphero obwerezabwereza, mapemphero opita kwa Mariya kapena kwa “oyera mtima” n’ngopanda pake

Tiyenera kupemphera kwa Mulungu m’dzina la Yesu. Yoh 14:6, 14; 16:23, 24

Mawu obwerezabwereza samvedwa. Mt 6:7

32. Sabata

A. Akhristu sakulamulidwa kusunga Sabata

Chilamulo chinathetsedwa pamaziko a imfa ya Yesu. Aef 2:15

Akhristu sakulamulidwa kusunga Sabata. Akl 2:16, 17; Aro 14:5, 10

Anadzudzulidwa chifukwa chosunga Sabata ndi zina zotero. Aga 4:9-11; Aro 10:2-4

Tiyenera kulowa mu mpumulo wa Mulungu mwa chikhulupiriro ndi kumvera. Ahe 4:9-11

B. Aisiraeli akale ndiwo okha anauzidwa kusunga Sabata

Sabata loyamba analisunga atayamba ulendo wawo waukulu. Eks 16:26, 27, 29, 30

Chinali chizindikiro chapadera kwa Aisiraeli. Eks 31:16, 17; Sl 147:19, 20

Chilamulo chinafunanso kuti azisunga zaka za Sabata. Eks 23:10, 11; Le 25:3, 4

Akhristu safunikira kusunga Sabata. Aro 14:5, 10; Aga 4:9-11

C. Sabata lopuma la Mulungu (tsiku la 7 la “mlungu” wolenga zinthu)

Linayamba atamaliza kulenga zinthu padziko lapansi. Ge 2:2, 3; Ahe 4:3-5

Linapitirira ngakhale pambuyo pa nthawi imene Yesu anali padziko lapansi. Ahe 4:6-8; Sl 95:7-9, 11

Akhristu amapuma pa ntchito zofuna kudzipindulitsa okha. Ahe 4:9, 10

Lidzatha Ufumu ukadzamaliza ntchito yake padziko lapansi. 1Ak 15:24, 28

33. Tchalitchi

A. Tchalitchi n’chauzimu, chomangidwa pa Khristu

Mulungu sakhala mu akachisi omangidwa ndi anthu. Mac 17:24, 25; 7:48

Tchalitchi choona ndicho kachisi wauzimu wa miyala yamoyo. 1Pe 2:5, 6

Khristu, mwala wa pakona. Atumwi, maziko achiwiri. Aef 2:20

Mulungu ayenera kulambiridwa ndi mzimu ndi choonadi. Yoh 4:24

B. Tchalitchi sichinamangidwe pa Petulo

Yesu sananene kuti tchalitchi chidzamangidwa pa Petulo. Mt 16:18

Yesu anatchulidwa kuti ndiye “thanthwe” limenelo. 1Ak 10:4

Petulo anati Yesu ndiye maziko. 1Pe 2:4, 6-8; Mac 4:8-12

34. Tchimo

A. Kodi tchimo n’chiyani?

Kuphwanya lamulo la Mulungu, kapena muyezo wake wangwiro. 1Yoh 3:4; 5:17

Munthu, pokhala cholengedwa cha Mulungu, ayenera kuyankha kwa iye. Aro 14:12; 2:12-15

Chilamulo chinadziwitsa uchimo, chinapangitsa anthu kuuzindikira. Aga 3:19; Aro 3:20

Tonse tili mu uchimo, ndife operewera pa muyezo wangwiro wa Mulungu. Aro 3:23; Sl 51:5

B. Chifukwa chimene tonse tikuvutikira ndi uchimo wa Adamu

Adamu anapatsira anthu onse kupanda ungwiro ndi imfa. Aro 5:12, 18

Mulungu anasonyeza chifundo polola anthu kukhalabe ndi moyo. Sl 103:8, 10, 14, 17

Nsembe ya Yesu imaphimba machimo. 1Yoh 2:2

Uchimo ndi ntchito zina zonse za Mdyerekezi zidzafafanizidwa. 1Yoh 3:8

C. Chipatso choletsedwa kunali kusamvera, sichinali kugonana

Lamulo loletsa kudya zipatso za mtengowo linaperekedwa Hava asanalengedwe. Ge 2:17, 18

Adamu ndi Hava anauzidwa kuti akhale ndi ana. Ge 1:28

Ana si chipatso cha uchimo, koma ndi dalitso la Mulungu. Sl 127:3-5

Hava anachimwa mwamuna wake ali kwina, iye ndiye anayamba kudya. Ge 3:6; 1Ti 2:11-14

Adamu, monga mutu, anapandukira lamulo la Mulungu. Aro 5:12, 19

D. Kodi kuchimwira mzimu n’chiyani? (Mt 12:32; Mko 3:28, 29)

Si tchimo lobadwa nalo ayi. Aro 5:8, 12, 18; 1Yoh 5:17

Munthu angamvetse chisoni mzimu woyera, n’kudzasintha. Aef 4:30; Yak 5:19, 20

Kuchita tchimo dala mobwerezabwereza kumabweretsa imfa. 1Yoh 3:6-9

Mulungu ndiye amaweruza oterowo, amawachotsera mzimu wake. Ahe 6:4-8

Sitiyenera kupempherera anthu osalapa oterowo. 1Yoh 5:16, 17

35. Ubatizo

A. Ndi wofunika kuti munthu akhale Mkhristu

Yesu anapereka chitsanzo. Mt 3:13-15; Ahe 10:7

N’chizindikiro cha kudzikana kapena kudzipereka kwa Mulungu. Mt 16:24; 1Pe 3:21

Ndi wa okhawo a msinkhu woti n’kuphunzitsidwa. Mt 28:19, 20; Mac 2:41

Kumizidwa m’madzi ndiko njira yoyenera. Mac 8:38, 39; Yoh 3:23

B. Suchotsa machimo

Yesu sanabatizidwe kuti achotse machimo. 1Pe 2:22; 3:18

Magazi a Yesu ndiwo amachotsa machimo. 1Yoh 1:7

36. Ufumu

A. Zimene Ufumu wa Mulungu udzachitire anthu

Udzakwaniritsa chifuniro cha Mulungu. Mt 6:9, 10; Sl 45:6; Chv 4:11

Ndi boma lokhala ndi mfumu ndi malamulo. Yes 9:6, 7; 2:3; Sl 72:1, 8

Udzachotsa zoipa zonse, udzalamulira dziko lonse lapansi. Da 2:44; Sl 72:8

Ulamuliro wa zaka 1,000 udzakonzanso anthu. Udzakonzanso Paradaiso. Chv 21:2-4; 20:6

B. Uyamba kugwira ntchito adani a Khristu akadalipo

Khristu ataukitsidwa anayembekeza kwa nthawi yaitali. Sl 110:1; Ahe 10:12, 13

Analandira mphamvu, anamenya nkhondo yolimbana ndi Satana. Sl 110:2; Chv 12:7-9; Lu 10:18

Ufumu unakhazikitsidwa pa nthawiyo, kenako padziko lapansi panagwa masoka. Chv 12:10, 12

Mavuto alipowa akutanthauza kuti ndi nthawi yoti tiime kumbali ya Ufumu. Chv 11:15-18

C. Suli ‘m’mitima,’ sunapangidwe ndi khama la anthu

Ufumuwo uli kumwamba, osati padziko lapansi. 2Ti 4:18; 1Ak 15:50; Sl 11:4

Suli ‘m’mitima,’ Yesu anali kulankhula kwa Afarisi. Lu 17:20, 21

Si mbali ya dziko lapansi. Yoh 18:36; Lu 4:5-8; Da 2:44

Maboma, mfundo zimene dzikoli limatsatira, zidzalowedwa m’malo. Da 2:44

37. Ukwati

A. Mgwirizano wa ukwati uyenera kukhala wolemekezeka

Umayerekezedwa ndi Khristu ndi mkwatibwi wake. Aef 5:22, 23

Pogona anthu okwatirana pasaipitsidwe. Ahe 13:4

Okwatirana akulangizidwa kusapatukana. 1Ak 7:10-16

Dama ndilo maziko okhawo a m’Malemba othetsera ukwati. Mt 19:9

B. Mfundo ya umutu iyenera kulemekezedwa ndi Akhristu

Monga mutu, mwamuna ayenera kukonda ndi kusamalira banja. Aef 5:23-31

Mkazi azigonjera, kukonda, ndi kumvera mwamuna wake. 1Pe 3:1-7; Aef 5:22

Ana akhale omvera. Aef 6:1-3; Akl 3:20

C. Udindo wa makolo achikhristu kwa ana awo

Kuwasonyeza chikondi, kukhala ndi nthawi yochita nawo zinthu, ndi kuwasamala. Tit 2:4

Musawakwiyitse. Akl 3:21

Muziwapezera zofunika, kuphatikizapo zinthu zauzimu. 2Ak 12:14; 1Ti 5:8

Aphunzitseni kuti adzathe kukhala ndi moyo wabwino. Aef 6:4; Miy 22:6, 15; 23:13, 14

D. Akhristu ayenera kukwatira Akhristu anzawo okha

Kwatirani “mwa Ambuye” basi. 1Ak 7:39; De 7:3, 4; Ne 13:26

E. Mitala siloledwa ndi Malemba

Dongosolo loyambirira linali lakuti mwamuna azikhala ndi mkazi mmodzi yekha. Ge 2:18, 22-25

Yesu anabwezeretsa muyezo umenewu kwa Akhristu. Mt 19:3-9

Akhristu oyambirira sanali kukwatira mitala. 1Ak 7:2, 12-16; Aef 5:28-31

38. Utatu

A. Mulungu, Atate, ndi mmodzi, wamkulu koposa m’chilengedwe chonse

Mulungu sali atatu mwa mmodzi. De 6:4; Mki 2:10; Mko 10:18; Aro 3:29, 30

Mwana anachita kulengedwa, Mulungu analiko yekha pa chiyambi. Chv 3:14; Akl 1:15; Yes 44:6

Mulungu ndiye wolamulira chilengedwe chonse nthawi zonse. Afi 2:5, 6; Da 4:35

Mulungu ayenera kulemekezedwa kuposa wina aliyense. Afi 2:10, 11

B. Mwana anali wamng’ono kwa Atate asanabwere padziko lapansi ndi pambuyo pake

Mwanayo anali womvera pamene anali kumwamba, anatumidwa ndi Atate. Yoh 8:42; 12:49

Padziko lapansi anali womvera, Atate anali wamkulu. Yoh 14:28; 5:19; Ahe 5:8

Kumwamba anamukweza n’kumupatsa udindo wapamwamba, koma anakhalabe pansi pa Atate wake. Afi 2:9; 1Ak 15:28; Mt 20:23

Yehova ndiye mutu wa Khristu, ndiye Mulungu wake. 1Ak 11:3; Yoh 20:17; Chv 1:6

C. Umodzi wa Mulungu ndi Khristu

Nthawi zonse amakhala ogwirizana kwathunthu. Yoh 8:28, 29; 14:10

Umodzi, monga wa mwamuna ndi mkazi wake. Yoh 10:30; Mt 19:4-6

Okhulupirira onse afunika kukhala ndi umodzi ngati umenewo. Yoh 17:20-22; 1Ak 1:10

Kulambira Yehova yekha kudzera mwa Khristu kudzakhalako kosatha. Yoh 4:23, 24

D. Mzimu woyera wa Mulungu ndi mphamvu yake yogwira ntchito

Ndi mphamvu, osati munthu. Mt 3:16; Yoh 20:22; Mac 2:4, 17, 33

Si munthu wokhala kumwamba pamodzi ndi Mulungu ndi Khristu. Mac 7:55, 56; Chv 7:10

Umayendetsedwa ndi Mulungu kuti ukwaniritse zolinga zake. Sl 104:30; 1Ak 12:4-11

Otumikira Mulungu amaulandira, umawatsogolera. 1Ak 2:12, 13; Aga 5:16

39. Yehova, Mulungu

A. Dzina la Mulungu

“Mulungu” ndi dzina laulemu chabe. Ambuye wathu ali ndi dzina lake lenileni. 1Ak 8:5, 6

Timapemphera kuti dzina lake liyeretsedwe. Mt 6:9, 10

Yehova ndilo dzina la Mulungu. Sl 83:18; Eks 6:2, 3; 3:15; Yes 42:8

Lilimo m’Baibulo la King James Version pa Eks 6:3

(m’mawu a m’munsi m’Baibulo la Douay Version). Sl 83:18; Yes 12:2; 26:4

Yesu anadziwitsa dzinalo. Yoh 17:6, 26; 5:43; 12:12, 13, 28

B. Mulungu aliko

N’zosatheka kuona Mulungu n’kukhalabe ndi moyo. Eks 33:20; Yoh 1:18; 1Yoh 4:12

Kuona Mulungu kuti tikhulupirire n’kosafunikira. Ahe 11:1; Aro 8:24, 25; 10:17

Mulungu amadziwika ndi ntchito zake zooneka. Aro 1:20; Sl 19:1, 2

Kukwaniritsidwa kwa maulosi ndi umboni wakuti Mulungu alikodi. Yes 46:8-11

C. Makhalidwe a Mulungu

Mulungu ndi chikondi. 1Yoh 4:8, 16; Eks 34:6; 2Ak 13:11; Mik 7:18

Ndi wopambana mu nzeru. Yob 12:13; Aro 11:33; 1Ak 2:7

Ndi wolungama, amaweruza molungama. De 32:4; Sl 37:28

Ndi wamphamvuyonse. Yob 37:23; Chv 7:12; 4:11

D. Sikuti anthu onse amatumikira Mulungu mmodzi

Njira yooneka yabwino, sikuti imakhala yolondola nthawi zonse. Miy 16:25; Mt 7:21

Pali misewu iwiri, umodzi wokha ndi umene ukupita ku moyo. Mt 7:13, 14; De 30:19

Pali milungu yambiri, koma Mulungu woona ndi mmodzi yekha. 1Ak 8:5, 6; Sl 82:1

Kudziwa Mulungu woona n’kofunika kuti tipeze moyo. Yoh 17:3; 1Yoh 5:20

40. Yesu

A. Yesu ndi Mwana wa Mulungu ndiponso Mfumu yoikidwa

Iye ndi woyamba kubadwa wa Mulungu,

anamugwiritsa ntchito polenga zinthu zina zonse. Chv 3:14; Akl 1:15-17

Anatumizidwa kudzabadwa monga munthu kwa mkazi, anakhala wotsikirapo kwa angelo. Aga 4:4; Ahe 2:9

Anabadwa mwa mzimu wa Mulungu, anali ndi tsogolo lokakhala kumwamba. Mt 3:16, 17

Anamukweza n’kumupatsa udindo wapamwamba kuposa umene anali nawo asanadzakhale munthu. Afi 2:9, 10

B. Kukhulupirira mwa Yesu Khristu n’kofunika kuti tidzapulumuke

Khristu ndiye Mbewu yolonjezedwa ya Abulahamu. Ge 22:18; Aga 3:16

Yesu yekha ndiye Mkulu wa Ansembe, dipo. 1Yoh 2:1, 2; Ahe 7:25, 26; Mt 20:28

Moyo umapezeka mwa kudziwa Mulungu ndi Khristu, kumvera. Yoh 17:3; Mac 4:12

C. Si kukhulupirira mwa Yesu kokha kumene kumafunika

Kukhulupirira kuzikhala ndi ntchito zake. Yak 2:17-26; 1:22-25

Tiyenera kumvera malamulo, kugwira ntchito imene anagwira. Yoh 14:12, 15; 1Yoh 2:3

Sikuti onse otchula dzina la Ambuye adzalowa mu Ufumu. Mt 7:21-23

41. Zifaniziro

A. Kugwiritsa ntchito zifaniziro polambira n’kutonza Mulungu

N’zosatheka kupanga chifaniziro cha Mulungu. 1Yoh 4:12; Yes 40:18; 46:5; Mac 17:29

Akhristu amachenjezedwa za zifaniziro. 1Ak 10:14; 1Yoh 5:21

Mulungu ayenera kulambiridwa ndi mzimu ndi choonadi. Yoh 4:24

B. Kulambira zifaniziro kunabweretsa imfa kwa mtundu wa Isiraeli

Ayuda analetsedwa kulambira zifaniziro. Eks 20:4, 5

Sizimva, sizilankhula. Ozipanga adzafanana nazo. Sl 115:4-8

Zinakhala msampha, zinabweretsa chiwonongeko. Sl 106:36, 40-42; Yer 22:8, 9

C. Kulambira Mulungu kudzera m’zifaniziro n’kosaloledwa

Mulungu anakana kuti anthu azimulambira pogwiritsa ntchito zifaniziro. Yes 42:8

Mulungu yekha ndiye “Wakumva pemphero.” Sl 65:1, 2

42. Zoipa, Mavuto a m’Dziko

A. Amene amachititsa mavuto m’dziko

Ulamuliro woipa ndi umene ukuchititsa kuti zinthu zikhale zoipa masiku ano. Miy 29:2; 28:28

Wolamulira dziko lapansili ndi mdani wa Mulungu. 2Ak 4:4; 1Yoh 5:19; Yoh 12:31

Mdyerekezi amachititsa masoka, nthawi yamuthera. Chv 12:9, 12

Mdyerekezi akadzamangidwa, padzakhala mtendere wochuluka. Chv 20:1-3; 21:3, 4

B. Chifukwa chake Mulungu walola kuti zoipa zizichitika

Mdyerekezi anatsutsa zakuti anthu angakhulupirike kwa Mulungu. Yob 1:11, 12

Okhulupirika amapatsidwa mwayi wosonyeza kukhulupirika kwawo. Aro 9:17; Miy 27:11

Mdyerekezi wapezeka kuti ndi wabodza, nkhaniyo idzathetsedwa. Yoh 12:31

Okhulupirika adzalandira mphoto ya moyo wosatha. Aro 2:6, 7; Chv 21:3-5

C. Kutalika kwa nthawi ya mapeto ndi chifundo cha Mulungu

Monga m’masiku a Nowa, kuchenjeza kumatenga nthawi. Mt 24:14, 37-39

Mulungu sakuchedwa, koma akusonyeza chifundo. 2Pe 3:9; Yes 30:18

Baibulo limatithandiza kuti tisadzadzidzimutsidwe. Lu 21:36; 1At 5:4

Panopa yesetsani kupeza njira imene Mulungu wapereka yokutetezerani. Yes 2:2-4; Zef 2:3

D. Njira yothetsera mavuto a dziko sidzachokera kwa anthu

Anthu ali ndi mantha aakulu, athedwa nzeru. Lu 21:10, 11; 2Ti 3:1-5

Ufumu wa Mulungu ndi umene udzapambane, osati anthu. Da 2:44; Mt 6:10

Kuti mukhale ndi moyo, yesetsani kukhala pa mtendere ndi Mfumu panopa. Sl 2:9, 11, 12

43. Zolembedweratu

A. Mulungu sanalemberetu tsogolo la munthu

Cholinga cha Mulungu n’chotsimikizirika. Yes 55:11; Ge 1:28

Munthu aliyense payekha ali ndi mwayi wosankha kutumikira Mulungu. Yoh 3:16; Afi 2:12

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena