Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyimbo ya Solomo 3
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Nyimbo ya Solomo 3:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Sa 18:20; Nym 1:7

Nyimbo ya Solomo 3:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +2Mb 9:30
  • +Ne 8:16; Mlr 4:18

Nyimbo ya Solomo 3:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 130:6; Nym 5:7

Nyimbo ya Solomo 3:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 22:16
  • +Nym 2:7
  • +Nym 8:4

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2015, tsa. 31

    11/15/2006, ptsa. 18-19

    11/15/1987, ptsa. 24-25

Nyimbo ya Solomo 3:6

Mawu a M'munsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yer 2:2
  • +Eks 30:23, 34

Nyimbo ya Solomo 3:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 9:22

Nyimbo ya Solomo 3:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ne 4:22; Mla 5:12

Nyimbo ya Solomo 3:9

Mawu a M'munsi

  • *

    Limeneli linali bedi lochita kunyamula, limene anali kunyamulirapo munthu wolemekezeka.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 5:9

Nyimbo ya Solomo 3:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Miy 4:9
  • +2Sa 12:24; Miy 4:3
  • +Yes 62:5

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Nyimbo 3:11Sa 18:20; Nym 1:7
Nyimbo 3:22Mb 9:30
Nyimbo 3:2Ne 8:16; Mlr 4:18
Nyimbo 3:3Sl 130:6; Nym 5:7
Nyimbo 3:51Mf 22:16
Nyimbo 3:5Nym 2:7
Nyimbo 3:5Nym 8:4
Nyimbo 3:6Yer 2:2
Nyimbo 3:6Eks 30:23, 34
Nyimbo 3:71Mf 9:22
Nyimbo 3:8Ne 4:22; Mla 5:12
Nyimbo 3:91Mf 5:9
Nyimbo 3:11Miy 4:9
Nyimbo 3:112Sa 12:24; Miy 4:3
Nyimbo 3:11Yes 62:5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano (nwt)
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Nyimbo ya Solomo 3:1-11

Nyimbo ya Solomo

3 “Pabedi panga usiku, ndinaganizira za munthu amene mtima wanga umam’konda.+ Ndinalakalaka kumuona koma iye panalibe. 2 Chotero ndinati: ‘Ndidzuke ndikazungulire mumzinda,+ m’misewu ndi m’mabwalo a mumzinda,+ kuti ndikafunefune munthu amene mtima wanga umam’konda.’ Ndinam’funafuna koma sindinamupeze. 3 Alonda+ amene anali kuzungulira mumzindawo anandipeza, ndipo ine ndinawafunsa kuti: ‘Kodi amuna inu, mwamuonako munthu amene mtima wanga umam’konda?’ 4 Nditangowapitirira pang’ono, ndinam’peza munthu amene mtima wanga umam’konda. Ndinamugwira ndipo sindinafune kum’siya mpaka nditamubweretsa m’nyumba mwa mayi anga, m’chipinda chamkati cha mayi amene anali ndi pakati kuti ine ndibadwe. 5 Ndakulumbiritsani inu+ ana aakazi a ku Yerusalemu, pali mbawala zazikazi ndiponso pali mphoyo zakutchire,+ kuti musayese kudzutsa chikondi mwa ine mpaka pamene chikondicho chifunire.”+

6 “Kodi chinthu chikuchokera kuchipululuchi n’chiyani, chooneka ngati utsi wokwera m’mwamba, chonunkhira mafuta a mule, lubani,*+ ndi mtundu uliwonse wa zonunkhira za ufa za munthu wamalonda?”+

7 “Taonani! Ndi bedi la Solomo. Amuna 60 amphamvu ochokera mwa amuna amphamvu a Isiraeli alizungulira.+ 8 Onsewo atenga malupanga ndipo ndi ophunzitsidwa nkhondo. Aliyense wamangirira lupanga lake m’chiuno mwake kuti adziteteze ku zoopsa za usiku.”+

9 “Ndi bedi* limene Mfumu Solomo inadzipangira ndi mitengo ya ku Lebanoni.+ 10 Mizati yake ndi yasiliva. Motsamira mwake ndi mwagolide. Pokhalira pake ndi popangidwa ndi ubweya wa nkhosa wonyika mu utoto wofiirira. Mkati mwake, ana aakazi a ku Yerusalemu akongoletsamo posonyeza chikondi.”

11 “Inu ana aakazi a Ziyoni, pitani panja mukaone Mfumu Solomo itavala nkhata yamaluwa,+ imene mayi ake+ anailukira pa tsiku la ukwati wake, pa tsiku limene mtima wa mfumuyo unasangalala.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena