Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 21:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Choncho iwo anayamba kuwiringula kwa Mulungu+ ndiponso Mose,+ kuti: “Munatitulutsiranji m’dziko la Iguputo? Kodi mumafuna kuti tidzafere m’chipululu?+ Kuno chakudya kulibe, madzinso kulibe.+ Chakudya chonyansachi chafika potikola.”+

  • Deuteronomo 8:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Mungaiwale amene anakudyetsani mana+ m’chipululu, chakudya chimene makolo anu sanachidziwe, pofuna kukuphunzitsani kudzichepetsa+ ndi kuti akuyeseni kuti potsirizira pake akuchitireni zabwino.+

  • Yoswa 5:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Mana analeka kugwa pa tsikuli, pamene ana a Isiraeli anadya zokolola za m’dzikomo. Kuyambira pamenepo, mana sanagwenso pakati pa ana a Isiraeli.+ Chotero, chaka chimenechi n’chimene iwo anayamba kudya zokolola za m’dziko la Kanani.+

  • Yohane 6:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Makolo athu anadya mana+ m’chipululu, monga mmene Malemba amanenera kuti, ‘Anawapatsa chakudya chochokera kumwamba kuti adye.’”+

  • Yohane 6:58
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 58 Chimenechi ndiye chakudya chotsika kumwamba. N’chosiyana ndi chakudya chimene makolo anu anadya koma anamwalirabe. Iye wakudya chakudya ichi adzakhala ndi moyo kosatha.”+

  • 1 Akorinto 10:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ndiponso, onse anadya chakudya chimodzimodzi chauzimu,+

  • Aheberi 9:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Mmenemu munali chiwaya chagolide chofukizira nsembe,+ ndi likasa la pangano.+ Likasa lonseli linali lokutidwa ndi golide.+ M’likasamo munali mtsuko wagolide wokhala ndi mana.+ Munalinso ndodo ya Aroni imene inaphuka ija,+ komanso miyala yosema+ ya pangano.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena