Deuteronomo 28:53 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 53 Pamenepo udzadya chipatso cha mimba yako, mnofu wa ana ako aamuna ndi ana ako aakazi,+ amene Yehova Mulungu wako wakupatsa, chifukwa cha zovuta ndi nsautso zimene adani ako adzakupanikiza nazo. 2 Mafumu 6:29 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 29 Choncho tinaphika+ mwana wanga n’kumudya.+ Tsiku lotsatira ndinauza mayiyu kuti, ‘Bweretsa mwana wako timudye.’ Koma iye anakam’bisa.” Yeremiya 19:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Ndidzawachititsa kudya mnofu wa ana awo aamuna ndi ana awo aakazi. Aliyense adzadya mnzake, chifukwa cha zovuta ndi nsautso zimene adani awo ndiponso anthu amene akufuna moyo wawo adzawapanikiza nazo.”’+ Maliro 2:20 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 20 Inu Yehova, yang’anani kuti muone+ yemwe mwamulanga chotere.Kodi amayi azidya zipatso za mimba yawo, ana awo athanzi?+Kapena kodi wansembe ndi mneneri aziphedwa m’malo opatulika a Yehova?+ Maliro 4:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Ngakhale amayi, amene amakhala achifundo, afika pophika ana awo ndi manja awo.+Anawo akhala ngati chakudya chotonthoza anthu pa nthawi ya kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.+ Ezekieli 5:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 “‘“Choncho pakati pako, abambo adzadya ana awo+ ndipo ana adzadya abambo awo. Ine ndidzakulanga ndipo anthu ako onse otsala ndidzawabalalitsira kumphepo zonse zinayi.”’+
53 Pamenepo udzadya chipatso cha mimba yako, mnofu wa ana ako aamuna ndi ana ako aakazi,+ amene Yehova Mulungu wako wakupatsa, chifukwa cha zovuta ndi nsautso zimene adani ako adzakupanikiza nazo.
29 Choncho tinaphika+ mwana wanga n’kumudya.+ Tsiku lotsatira ndinauza mayiyu kuti, ‘Bweretsa mwana wako timudye.’ Koma iye anakam’bisa.”
9 Ndidzawachititsa kudya mnofu wa ana awo aamuna ndi ana awo aakazi. Aliyense adzadya mnzake, chifukwa cha zovuta ndi nsautso zimene adani awo ndiponso anthu amene akufuna moyo wawo adzawapanikiza nazo.”’+
20 Inu Yehova, yang’anani kuti muone+ yemwe mwamulanga chotere.Kodi amayi azidya zipatso za mimba yawo, ana awo athanzi?+Kapena kodi wansembe ndi mneneri aziphedwa m’malo opatulika a Yehova?+
10 Ngakhale amayi, amene amakhala achifundo, afika pophika ana awo ndi manja awo.+Anawo akhala ngati chakudya chotonthoza anthu pa nthawi ya kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.+
10 “‘“Choncho pakati pako, abambo adzadya ana awo+ ndipo ana adzadya abambo awo. Ine ndidzakulanga ndipo anthu ako onse otsala ndidzawabalalitsira kumphepo zonse zinayi.”’+