Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 28:38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Chotero kachitsuloko kazikhala pamphumi pa Aroni, ndipo Aroni aziyankha mlandu wa machimo ochimwira zinthu zopatulika,+ zimene ana a Isiraeli adzaziyeretsa. Izi ndizo mphatso zawo zonse zopatulika. Kachitsuloko kazikhala pamphumi pake nthawi zonse, kuti azichititsa anthuwo kukhala ovomerezeka+ pamaso pa Yehova.

  • Numeri 18:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Tsopano Yehova analankhula ndi Aroni kuti: “Iwe ndi ana ako, ndi nyumba yonse ya bambo ako, mudzasenza zolakwa zanu pa malamulo okhudza malo opatulika.+ Iweyo ndi ana ako mudzasenza zolakwa zanu pa malamulo okhudza unsembe wanu.+

  • Yesaya 53:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chifukwa cha kuvutika kwake, iye adzaona zabwino+ ndipo adzakhutira.+ Chifukwa cha zimene akudziwa, mtumiki wanga wolungamayo+ adzachititsa kuti anthu ambiri azionedwa olungama,+ ndipo adzasenza zolakwa zawo.+

  • Yohane 1:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Tsiku lotsatira anaona Yesu akubwera kwa iye, ndipo anati: “Taonani, Mwanawankhosa+ wa Mulungu amene akuchotsa uchimo+ wa dziko!+

  • 2 Akorinto 5:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Amene analibe uchimoyo,+ Mulungu anamupanga kukhala uchimo+ chifukwa cha ife, kuti tikhale olungama pamaso pa Mulungu+ kudzera mwa iye.

  • Aheberi 9:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 n’chimodzimodzinso Khristu. Iye anaperekedwa nsembe kamodzi+ kokha kuti anyamule machimo a anthu ambiri.+ Ndipo nthawi yachiwiri+ imene adzaonekere+ sadzaonekera n’cholinga chochotsa uchimo.+ Anthu amene akumuyembekezera ndi mtima wonse kuti awapulumutse ndi amene adzamuone.+

  • 1 Petulo 2:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Iye ananyamula machimo athu+ m’thupi lake pamtengo,+ kuti tilekane ndi machimo+ n’kukhala amoyo m’chilungamo. Ndipo “munachiritsidwa ndi mabala ake.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena