Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 20:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 “Usadzipangire fano kapena chifaniziro cha chinthu chilichonse chakumwamba, kapena chapadziko lapansi, kapenanso cham’madzi a padziko lapansi.*+

  • Levitiko 26:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 “‘Musadzipangire milungu yopanda pake,+ chifaniziro,+ kapena chipilala chopatulika. Musaike mwala wokhala ndi zithunzi zojambula mochita kugoba+ m’dziko lanu kuti muziugwadira,+ chifukwa ine ndine Yehova Mulungu wanu.

  • Deuteronomo 17:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 moti akupita kukalambira milungu ina ndi kuigwadira, kapena kugwadira dzuwa, mwezi kapena khamu lonse la zinthu zakuthambo,+ chinthu chimene ine sindinakulamuleni,+

  • Deuteronomo 27:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 “‘Wotembereredwa ndi munthu aliyense wopanga chifaniziro chosema+ kapena chifaniziro chopangidwa ndi chitsulo chosungunula+ ndi kuchibisa. Chifanizirocho ndi chinthu chonyansa kwa Yehova,+ Mulungu wopanga manja a mmisiri wa matabwa ndi zitsulo.’+ (Anthu onse ayankhe kuti, ‘Zikhale momwemo!’)*+

  • Oweruza 17:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Koma Mika anabweza ndalamazo kwa mayi ake, ndipo mayi akewo anatenga ndalama zasiliva zokwana 200 n’kuzipereka kwa wosula siliva.+ Pamenepo wosula silivayo anapanga chifaniziro chosema+ ndi chifaniziro chopangidwa ndi chitsulo chosungunula.+ Zinthu zimenezi anaziika m’nyumba ya Mika.

  • Oweruza 18:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Amuna asanuwo analowa m’nyumba ya Mika ndi kutenga chifaniziro chosema, efodi, aterafi ndi chifaniziro chopangidwa ndi chitsulo chosungunula.+ Atatero wansembeyo+ anawafunsa kuti: “Mukutani kodi?”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena