Genesis 34:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Kuwayankha kwake anati: “Sitingachite zimenezo. Sitingapereke mlongo wathu kwa mwamuna wosadulidwa.+ Zimenezo n’zonyazitsa kwa ife. 1 Samueli 14:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Choncho Yonatani anauza mtumiki wake womunyamulira zida uja kuti: “Tiye tiwolokere kumudzi wa amuna osadulidwawa.+ Pakuti mwina Yehova adzatithandiza, chifukwa palibe chimene chingalepheretse Yehova kupulumutsa anthu ake pogwiritsa ntchito anthu ambiri kapena ochepa.”+ 1 Samueli 17:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 Ndiyeno Davide anayamba kufunsa amuna amene anali ataimirira pafupi naye kuti: “Kodi munthu amene angakaphe Mfilisiti+ ameneyu ndi kuchotsa chitonzo pa Isiraeli+ amuchitira chiyani? Kodi Mfilisiti wosadulidwa+ ameneyu ndani kuti azinyoza+ asilikali a Mulungu wamoyo?”+ 1 Samueli 31:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Kenako Sauli anauza womunyamulira zida kuti: “Solola lupanga lako+ undibaye* nalo, kuti amuna osadulidwawa+ asandipeze ndi kundibaya komanso kundizunza.” Koma womunyamulira zida uja sanafune,+ chifukwa anali kuopa kwambiri. Chotero Sauli anatenga lupanga lake ndi kuligwera.+ 2 Samueli 1:20 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 20 Anthu inu musanene zimenezi mumzinda wa Gati.+Musalengeze zimenezi m’misewu ya Asikeloni,+Kuopera kuti ana aakazi a Afilisiti angasangalale,+Kuopera kuti ana aakazi a anthu osadulidwa angakondwere.
14 Kuwayankha kwake anati: “Sitingachite zimenezo. Sitingapereke mlongo wathu kwa mwamuna wosadulidwa.+ Zimenezo n’zonyazitsa kwa ife.
6 Choncho Yonatani anauza mtumiki wake womunyamulira zida uja kuti: “Tiye tiwolokere kumudzi wa amuna osadulidwawa.+ Pakuti mwina Yehova adzatithandiza, chifukwa palibe chimene chingalepheretse Yehova kupulumutsa anthu ake pogwiritsa ntchito anthu ambiri kapena ochepa.”+
26 Ndiyeno Davide anayamba kufunsa amuna amene anali ataimirira pafupi naye kuti: “Kodi munthu amene angakaphe Mfilisiti+ ameneyu ndi kuchotsa chitonzo pa Isiraeli+ amuchitira chiyani? Kodi Mfilisiti wosadulidwa+ ameneyu ndani kuti azinyoza+ asilikali a Mulungu wamoyo?”+
4 Kenako Sauli anauza womunyamulira zida kuti: “Solola lupanga lako+ undibaye* nalo, kuti amuna osadulidwawa+ asandipeze ndi kundibaya komanso kundizunza.” Koma womunyamulira zida uja sanafune,+ chifukwa anali kuopa kwambiri. Chotero Sauli anatenga lupanga lake ndi kuligwera.+
20 Anthu inu musanene zimenezi mumzinda wa Gati.+Musalengeze zimenezi m’misewu ya Asikeloni,+Kuopera kuti ana aakazi a Afilisiti angasangalale,+Kuopera kuti ana aakazi a anthu osadulidwa angakondwere.