-
2 Mbiri 14:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Asa anachita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wake.
-
-
2 Mbiri 14:11Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
11 Tsopano Asa anayamba kupemphera kwa Yehova Mulungu wake,+ kuti: “Inu Yehova mukafuna kuthandiza, zilibe kanthu kuti anthuwo ndi ambiri kapena ndi opanda mphamvu.+ Tithandizeni Yehova Mulungu wathu chifukwa tikudalira inu,+ ndipo tabwera m’dzina lanu+ kudzamenyana ndi khamuli. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu.+ Musalole kuti munthu akuposeni mphamvu.”+
-
-
2 Mbiri 15:8Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
8 Asa atangomva mawu amenewa ndi ulosi wa mneneri Odedi,+ analimba mtima n’kuyamba kuchotsa zinthu zonyansa+ m’dziko lonse la Yuda ndi Benjamini ndi m’mizinda imene analanda m’dera lamapiri la Efuraimu.+ Anayambanso kukonza guwa lansembe la Yehova limene linali patsogolo pa khonde la nyumba ya Yehova.+
-