Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 7:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Pakuti adzapatutsa ana ako aamuna kuti asanditsatire ndipo adzatumikira ndithu milungu ina.+ Pamenepo mkwiyo wa Yehova udzakuyakirani ndipo adzakuwonongani ndithu mofulumira.+

  • 1 Mafumu 7:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Kenako Solomo anamanga nyumba yake yokhalamo kubwalo lina+ chapatali ndi nyumba ya Bwalo la Mpando Wachifumu. Kamangidwe ka nyumbayi kanali kofanana ndi ka Bwalo la Mpando Wachifumu. Panalinso nyumba ina yofanana ndi Bwaloli imene Solomo anamangira mwana wamkazi wa Farao+ amene iye anam’kwatira.

  • 1 Mafumu 9:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Mwana wamkazi wa Farao+ anachoka ku Mzinda wa Davide+ n’kukakhala kunyumba yake imene Solomo anam’mangira. Panali pa nthawi imeneyi pamene Solomo anamanga Chimulu cha Dothi.*+

  • 1 Mafumu 11:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Mfumu Solomo inakonda akazi ambiri achilendo+ kuphatikiza pa mwana wamkazi wa Farao.+ Inakonda akazi achimowabu,+ achiamoni,+ achiedomu,+ achisidoni,+ ndi achihiti.+

  • Ezara 10:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Patapita nthawi wansembe Ezara anaimirira n’kuuza anthuwo kuti: “Inuyo mwachita zosakhulupirika chifukwa mwatenga akazi achilendo+ n’kuwonjezera pa machimo a Isiraeli.+

  • Nehemiya 13:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Kodi si zodabwitsa kuti inunso mukuchita choipa chachikulu chimenechi, mwa kukwatira akazi achilendo, kumene ndi kuchita mosakhulupirika kwa Mulungu wanu?”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena