-
Yeremiya 37:21Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
21 Chotero Mfumu Zedekiya inalamula kuti atsekere Yeremiya m’Bwalo la Alonda+ ndipo anali kumupatsa mtanda wobulungira wa mkate tsiku ndi tsiku. Mkate umenewu unali kuchokera kumsewu wa ophika mkate+ ndipo anapitiriza kum’patsa mkatewo kufikira mkate wonse utatha mumzindamo.+ Choncho Yeremiya anapitiriza kukhala m’Bwalo la Alonda.+
-
-
Ezekieli 5:12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
12 Gawo limodzi la magawo atatu a anthu a mtundu wako adzafa ndi mliri+ ndipo adzatha ndi njala pakati pako.+ Gawo lina la magawo atatu a anthu a mtundu wako adzaphedwa ndi lupanga mokuzungulira. Gawo lomaliza la magawo atatu a anthu a mtundu wako ndidzawabalalitsira kumphepo zonse zinayi,+ ndipo ndidzawatsatira nditasolola lupanga.+
-