Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 32:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Pamenepo Mose anagawira malo ana a Gadi+ ndi ana a Rubeni.+ Anagawiranso malo hafu ya fuko la Manase+ mwana wa Yosefe. Anawagawira malo a ufumu wa Sihoni+ mfumu ya Aamori, ndi a ufumu wa Ogi+ mfumu ya Basana, dera lonse la mizinda ndi midzi yozungulira.

  • Deuteronomo 3:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Choncho pa nthawi imeneyo tinatenga dzikoli kukhala lathu. Mafuko a Rubeni ndi Gadi+ ndinawapatsa Aroweli,+ mzinda umene uli m’chigwa cha Arinoni, ndi hafu ya dera lamapiri la Giliyadi, ndi mizinda yake.

  • Yoswa 12:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Tsopano awa ndi mafumu amene ana a Isiraeli anagonjetsa n’kulanda madera awo, kumbali yotulukira dzuwa+ ya mtsinje wa Yorodano. Analanda kuchokera kuchigwa* cha Arinoni+ kukafika kuphiri la Herimoni+ ndi ku Araba+ konse, kumbali yotulukira dzuwa. Mafumu ake ndi awa:

  • Nehemiya 9:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 “Pamenepo munawapatsa maufumu+ ndi mitundu ya anthu ndipo munawagawira dzikolo chigawo ndi chigawo.+ Iwo anatenga dziko la Sihoni,+ dziko la mfumu ya Hesiboni+ ndi dziko la Ogi+ mfumu ya Basana.+

  • Salimo 44:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  2 Munapitikitsa anthu a mitundu ina ndi dzanja lanu,+

      Ndipo m’malo mwawo munakhazikitsa anthu anu.+

      Munagonjetsa mitundu ya anthu ndi kuipitikitsa.+

  • Salimo 78:55
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 55 Chifukwa cha iwo anachotsa mitundu ina pang’onopang’ono m’dzikoli,+

      Ndipo anayesa dzikoli ndi kuligawa kwa iwo kukhala cholowa chawo,+

      Moti anachititsa mafuko a Isiraeli kukhala m’nyumba zawozawo.+

  • Salimo 105:44
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Pang’onopang’ono anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina,+

      Ndipo zipatso za ntchito imene mitundu ya anthu inagwira mwakhama, anazitenga kukhala zawo,+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena