Deuteronomo 15:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 “Wina mwa abale ako akasauka pakati panu, mu umodzi mwa mizinda yanu, m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa, usamuumire mtima kapena kumuumitsira dzanja lako.+ Salimo 41:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 41 Wodala ndi munthu amene amachita zinthu moganizira munthu wonyozeka.+Pa tsiku la tsoka, Yehova adzamupulumutsa.+ Miyambo 14:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Munthu wonyoza mnzake ndiye kuti akuchimwa,+ koma wodala ndi munthu wokomera mtima anthu osautsika.+ Miyambo 19:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Wokomera mtima munthu wonyozeka akukongoza Yehova,+ ndipo adzam’bwezera zimene anachitazo.+ Miyambo 22:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Wa diso labwino adzadalitsidwa, chifukwa amapereka chakudya chake kwa munthu wonyozeka.+ Yesaya 58:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Ndimafunanso kuti muzigawira chakudya chanu anthu anjala,+ ndiponso kuti muziitanira m’nyumba zanu anthu osautsika ndi osowa pokhala.+ Ndimafuna kuti mukaona munthu wosavala muzimuveka+ ndiponso kuti musamadzibise kwa abale anu.+ 2 Akorinto 9:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Koma ponena za nkhaniyi, wobzala moumira+ adzakololanso zochepa, ndipo wobzala mowolowa manja+ adzakololanso zochuluka. Aheberi 13:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Komanso, musaiwale kuchita zabwino+ ndi kugawana zinthu ndi ena, pakuti nsembe zotero Mulungu amakondwera nazo.+
7 “Wina mwa abale ako akasauka pakati panu, mu umodzi mwa mizinda yanu, m’dziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa, usamuumire mtima kapena kumuumitsira dzanja lako.+
41 Wodala ndi munthu amene amachita zinthu moganizira munthu wonyozeka.+Pa tsiku la tsoka, Yehova adzamupulumutsa.+
21 Munthu wonyoza mnzake ndiye kuti akuchimwa,+ koma wodala ndi munthu wokomera mtima anthu osautsika.+
7 Ndimafunanso kuti muzigawira chakudya chanu anthu anjala,+ ndiponso kuti muziitanira m’nyumba zanu anthu osautsika ndi osowa pokhala.+ Ndimafuna kuti mukaona munthu wosavala muzimuveka+ ndiponso kuti musamadzibise kwa abale anu.+
6 Koma ponena za nkhaniyi, wobzala moumira+ adzakololanso zochepa, ndipo wobzala mowolowa manja+ adzakololanso zochuluka.
16 Komanso, musaiwale kuchita zabwino+ ndi kugawana zinthu ndi ena, pakuti nsembe zotero Mulungu amakondwera nazo.+