Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 28:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 Mitembo yanu idzakhala chakudya cha cholengedwa chilichonse chouluka m’mlengalenga ndi zilombo zakutchire, ndipo sipadzakhala woziopsa.+

  • 1 Mafumu 14:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Munthu wa m’banja la Yerobowamu wofera mumzinda, agalu adzamudya,+ ndipo wofera kuthengo, mbalame zam’mlengalenga zidzamudya,+ chifukwa choti Yehova wanena.”’

  • Salimo 79:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  2 Apereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame kuti chikhale chakudya chawo.+

      Matupi a okhulupirika anu awapereka kwa zilombo zakutchire.+

  • Yeremiya 7:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Mitembo ya anthu awa idzakhala chakudya cha zolengedwa zouluka zam’mlengalenga ndi cha zilombo zakutchire, ndipo sipadzakhala woziopsa.+

  • Yeremiya 16:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 ‘Iwo adzafa ndi matenda oopsa+ ndipo sadzawalira maliro+ kapena kuikidwa m’manda+ koma adzakhala ngati manyowa panthaka.+ Iwo adzafa ndi lupanga ndiponso njala yaikulu.+ Mitembo yawo idzakhala chakudya cha zolengedwa zouluka zam’mlengalenga ndi zilombo zakutchire.’+

  • Yeremiya 19:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ndidzasokoneza zolinga za Yuda ndi za Yerusalemu m’malo ano,+ ndipo ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga la adani awo komanso ndi anthu amene akufunafuna moyo wawo.+ Mitembo yawo ndidzaipereka kwa zolengedwa zouluka zam’mlengalenga ndi zilombo zakutchire kuti ikhale chakudya chawo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena