3 Tsopano iwo akunena kuti: “‘Kodi ifeyo tinavutikiranji kusala kudya inu osaona,+ ndipo tinadzisautsiranji+ inu osasamala n’komwe?’+
“Komatu anthu inu munali kusangalala tsiku limene munali kusala kudya, pamene antchito anu onse munali kuwagwiritsa ntchito yakalavulagaga.+