Yeremiya 2:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Ansembe sanafunse kuti, ‘Ali kuti Yehova?’+ Ndipo anthu ophunzitsa chilamulo sanandidziwe.+ Abusa nawonso anaphwanya malamulo anga,+ ndipo aneneri anali kulosera m’dzina la Baala+ ndi kutsatira milungu yopanda phindu.+ Yeremiya 5:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 “Iwo akana Yehova, ndipo akunena kuti, ‘Iye kulibe.+ Ndipo ife tsoka silidzatigwera. Sitidzaona lupanga lililonse kapena njala yaikulu.’+ Yeremiya 5:31 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 31 Aneneri akulosera monama,+ ndipo ansembe akupondereza anthu ndi mphamvu zawo.+ Anthu anga nawonso akukonda zimenezi.+ Ndipo kodi anthu inu mudzachita chiyani pamapeto pake?”+ Yeremiya 23:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Yehova wa makamu wanena kuti: “Musamvere mawu a aneneri amene akulosera kwa anthu inu.+ Akukulimbikitsani kuchita zinthu zopanda pake.+ Iwo akulankhula masomphenya a mumtima mwawo+ osati ochokera m’kamwa mwa Yehova.+ Yeremiya 27:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Anthu inu musamvere mawu a aneneri amene akukuuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya Babulo,’+ chifukwa zimene akulosera kwa inuzo ndi zonama.+ Yeremiya 29:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Pakuti ‘zimene akukuuzanizo akulosera m’dzina langa monama. Ine sindinawatume,’+ watero Yehova.”’” Ezekieli 13:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 “Iwe mwana wa munthu, losera zokhudza aneneri a mu Isiraeli.+ Uuze amene akulosera zam’mutu mwawo+ kuti, ‘Mvetserani mawu a Yehova.+
8 Ansembe sanafunse kuti, ‘Ali kuti Yehova?’+ Ndipo anthu ophunzitsa chilamulo sanandidziwe.+ Abusa nawonso anaphwanya malamulo anga,+ ndipo aneneri anali kulosera m’dzina la Baala+ ndi kutsatira milungu yopanda phindu.+
12 “Iwo akana Yehova, ndipo akunena kuti, ‘Iye kulibe.+ Ndipo ife tsoka silidzatigwera. Sitidzaona lupanga lililonse kapena njala yaikulu.’+
31 Aneneri akulosera monama,+ ndipo ansembe akupondereza anthu ndi mphamvu zawo.+ Anthu anga nawonso akukonda zimenezi.+ Ndipo kodi anthu inu mudzachita chiyani pamapeto pake?”+
16 Yehova wa makamu wanena kuti: “Musamvere mawu a aneneri amene akulosera kwa anthu inu.+ Akukulimbikitsani kuchita zinthu zopanda pake.+ Iwo akulankhula masomphenya a mumtima mwawo+ osati ochokera m’kamwa mwa Yehova.+
14 Anthu inu musamvere mawu a aneneri amene akukuuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya Babulo,’+ chifukwa zimene akulosera kwa inuzo ndi zonama.+
2 “Iwe mwana wa munthu, losera zokhudza aneneri a mu Isiraeli.+ Uuze amene akulosera zam’mutu mwawo+ kuti, ‘Mvetserani mawu a Yehova.+