Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 3:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 “Ndiyeno chidzachitike n’chakuti, m’malo mwa mafuta a basamu onunkhira+ padzangokhala fungo loipa, m’malo mwa lamba padzakhala chingwe, m’malo mwa tsitsi lokonzedwa bwino padzakhala mpala,+ m’malo mwa chovala chamtengo wapatali munthu adzavala chiguduli,*+ ndipo padzakhala chipsera*+ m’malo mwa kukongola.

  • Yesaya 15:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Anthu avala ziguduli+ m’misewu yake. Pamadenga*+ ake ndi m’mabwalo a mizinda yake, aliyense akufuula. Akulira n’kumapita kumunsi.+

  • Yeremiya 48:37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Mutu uliwonse wametedwa mpala,+ ndipo ndevu zonse n’zometa.+ M’manja monse ndi mochekekachekeka,+ ndipo anthu onse amanga ziguduli m’chiuno mwawo.’”+

  • Amosi 8:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndidzasandutsa zikondwerero zanu kukhala maliro+ ndipo nyimbo zanu zonse zidzakhala nyimbo zoimba polira. Ndidzachititsa kuti anthu onse avale ziguduli* ndipo mitu yonse idzametedwa mpala.+ Ndidzachititsa kuti zochitika pa tsikulo zikhale ngati maliro a mwana wamwamuna mmodzi yekhayo amene wamwalira,+ moti tsiku la mapeto a zinthu zonsezi lidzakhala lowawa.’

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena