1M’chaka choyamba cha Koresi+ mfumu ya Perisiya, Yehova analimbikitsa+ mtima wa Koresi mfumu ya Perisiya kuti mawu a Yehova kudzera mwa Yeremiya+ akwaniritsidwe. Pamenepo Koresiyo anatumiza mawu amene analengezedwa+ mu ufumu wake wonse. Mawuwo analembedwanso m’makalata,+ kuti:
5 Ndiyeno atsogoleri+ a mabanja a fuko la Yuda, la Benjamini, ansembe, ndi Alevi, aliyense amene Mulungu woona analimbikitsa mtima wake,+ ananyamuka kuti apite kukamanganso nyumba ya Yehova,+ yomwe inali ku Yerusalemu.