10 M’tsiku limenelo,+ padzakhala muzu wa Jese+ womwe udzaimirire ngati chizindikiro kwa anthu.+ Ngakhale anthu a mitundu ina adzatembenukira kwa iye kuti awatsogolere,+ ndipo malo ake okhalapo adzakhala aulemerero.+
21 Koma ndachitira umboni mokwanira+ kwa Ayuda ndi kwa Agiriki omwe, kuti alape+ ndi kutembenukira kwa Mulungu, komanso kuti akhale ndi chikhulupiriro mwa Ambuye wathu Yesu.