Aroma
10 Ndithu abale, chimene ndikufunitsitsa mumtima mwanga ndiponso pembedzero langa kwa Mulungu ndi lakuti Aisiraeli apulumutsidwe.+ 2 Pakuti ndikuwachitira umboni kuti ndi odzipereka+ potumikira Mulungu, koma samudziwa molondola.+ 3 Ndipo posadziwa chilungamo cha Mulungu,+ iwo sanagonjere chilungamocho+ koma anayesetsa kukhazikitsa chawochawo.+ 4 Pakuti Khristu ndiye kutha kwa Chilamulo,+ kuti aliyense wokhulupirira akhale wolungama.+
5 Pajatu Mose analemba kuti munthu wochita chilungamo cha m’Chilamulo adzakhala ndi moyo chifukwa cha chilungamo chimenecho.+ 6 Koma za chilungamo chimene chimabwera chifukwa cha chikhulupiriro, Malemba amati: “Mumtima mwako usanene kuti,+ ‘Kodi ndani adzakwera kumwamba?’+ kuti akatsitse Khristu.+ 7 Kapena, ‘Kodi ndani adzatsikira kuphompho?’+ kuti akaukitse Khristu kwa akufa.”+ 8 Koma kodi Lemba limati chiyani? Limati: “Mawu a chilamulowo ali pafupi ndi iwe, ali m’kamwa mwako ndi mumtima mwako,”+ amenewa ndi “mawu”+ a chikhulupiriro, amene tikulalikira.+ 9 Pakuti ngati ukulengeza kwa anthu ‘mawu amene ali m’kamwa mwakowo,’+ akuti Yesu ndiye Ambuye,+ ndipo mumtima mwako ukukhulupirira kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa,+ udzapulumuka.+ 10 Munthu amakhala ndi chikhulupiriro mumtima mwake+ kuti akhale wolungama, koma ndi pakamwa pake amalengeza poyera+ chikhulupiriro chake kuti apulumuke.
11 Paja Lemba limati: “Palibe wokhulupirira iye,+ amene adzakhumudwe.”+ 12 Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi Mgiriki,+ popeza kwa onsewo Ambuye ndi mmodzi, amene amapereka mowolowa manja+ kwa onse oitana pa dzina lake. 13 Pakuti “aliyense amene adzaitana pa dzina la Yehova* adzapulumuka.”+ 14 Komabe, kodi angaitane bwanji munthu amene samukhulupirira?+ Angakhulupirire bwanji munthu amene sanamvepo za iye? Angamve bwanji za iye popanda wina kulalikira?+ 15 Ndipo angalalikire bwanji ngati sanatumidwe?+ Zili monga muja Malemba amanenera kuti: “Mapazi a anthu olengeza uthenga wabwino wa zinthu zabwino, ndi okongola kwabasi!”+
16 Ngakhale zili choncho, si onse amene analabadira uthenga wabwino.+ Pakuti Yesaya anati: “Yehova, kodi ndani wakhulupirira zimene anamva kwa ife?”+ 17 Chotero munthu amakhala ndi chikhulupiriro chifukwa cha zimene wamva.+ Ndipo zimene wamvazo zimachokera m’mawu onena za Khristu.+ 18 Koma ndifunsebe kuti, Kodi kumva sanamve? Pajatu “liwu lawo linamveka padziko lonse lapansi,+ ndipo mawu awo anamveka kumalekezero a dziko lapansi kumene kuli anthu.”+ 19 Komabe ndifunse kuti, Kodi si zoona kuti Aisiraeli anadziwa?+ Choyamba Mose anati: “Ndidzakuchititsani nsanje kudzera mwa anthu omwe si mtundu. Ndidzaputa mkwiyo wanu woopsa kudzera mwa mtundu wopusa.”+ 20 Koma Yesaya analankhula molimba mtima kwambiri kuti: “Anthu amene anandipeza ndi amene sanali kundifunafuna.+ Ndinaonekera kwa anthu amene sanafunse za ine kuti andipeze.”+ 21 Koma za Aisiraeli iye anati: “Ndatambasula manja anga tsiku lonse kwa anthu osamva+ komanso otsutsa.”+